< 1 Cronicas 16 >

1 Inserrekda ti lakasa ti tulag ti Dios ket inkabilda daytoy iti tengnga ti tolda nga impatakder ni David para iti daytoy. Ket nagidatagda kadagiti daton a mapuoran ken daton a pakikappia iti sangoanan ti Dios.
Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
2 Idi nalpasen nga indatag ni David dagiti daton a mapuoran ken daton a pakikappia, binendisionanna dagiti tattao iti nagan ni Yahweh.
Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
3 Binunonganna ti tunggal Israelita, babbai ken lallaki, iti saggaysa a tinapay, karne ken kankanen a naaramid iti pasas.
Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
4 Nangdutok ni David kadagiti sumagmamano a Levita nga agserbi iti sangoanan ti lakasa ti tulag ni Yahweh, ken tapno agrambak, agyaman ken agdayaw kenni Yahweh a Dios ti Israel.
Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
5 Dagitoy a Levita ket da Asaf nga isu ti mangidadaulo, ken ti sumaruno kenkuana ket da Zecarias, Jeiel, Semiramot, Jehiel, Mattitias, Eliab, Benaias, Obed Edom ken Jeiel. Isuda ti mangtukar kadagiti instrumento a nakuerdasan ken kadagiti arpa. Ni Asaf ti mangpaaweng iti napigsa kadagiti piangpiang.
Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
6 Da Benaias ken Jahaziel a papadi ti mangpuyot a kanayon kadagiti tangguyob, iti sangoanan ti lakasa ti tulag ti Dios.
ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
7 Ket iti dayta nga aldaw, dinutokan nga immuna ni David ni Asaf ken dagiti kakabsatna a lallaki nga agkanta iti kanta a pagyaman kenni Yahweh.
Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
8 Agyamankayo kenni Yahweh, umawagkayo ti naganna; ipakaammoyo dagiti aramidna kadagiti nasion.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
9 Kaantaanyo isuna, kantaanyo isuna iti kanta a pagdayaw; ibagayo dagiti amin a nakaskasdaaw nga aramidna.
Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
10 Ipasindayawyo ti nasantoan a naganna; agrag-o koma ti puso dagiti mangbirok kenni Yahweh.
Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
11 Birukenyo ni Yahweh ken ti pigsana; birukenyo a kanayon ti presensiana.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
12 Lagipenyo dagiti nakaskasdaaw a banbanag nga inaramidna, dagiti milagro ken dagiti bilin a nagtaud iti ngiwatna,
Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
13 dakayo a kaputotan ni Israel nga adipenna, dakayo a tattao ni Jacob, a pinilina.
inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
14 Isuna ni Yahweh a Diostayo. Ti bilinna ket adda iti entero a daga.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
15 Panunotenyo iti agnanayon ti katulaganna, ti sao nga imbilinna iti sangaribu a henerasion.
Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
16 Laglagipenna ti katulaganna kenni Abraham, ken ti sapatana kenni Isaac.
pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
17 Daytoy ti pinatalgedanna kenni Jacob a kas alagaden, ken iti Israel a kas agnanayon a katulagan.
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
18 Kinunana, “Itedkonto kadakayo ti daga ti Canaan a kas bingayyo iti tawidyo.”
“Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
19 Imbagak daytoy idi bassit pay laeng ti bilangyo, bassitkayo unay, ken ganggannaetkayo iti daga.
Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
20 Nagakar-akarda kadagiti nasion, nagakar-akarda kadagiti pagarian.
iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
21 Saanna a pinalubosan ti siasinoman a mangidadanes kadakuada; dinusana dagiti ar-ari para iti pagsayaatanda,
Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
22 kinunana, “Saanyo a sagiden dagiti pinulotak, ken saanyo a dangran dagiti propetak.”
“Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
23 Kaantaanyo ni Yahweh, dakayo nga entero a daga; iwaragawagyo ti panangisalakanna iti inaldaw-aldaw.
Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
24 Ipakaammoyo ti dayagna kadagiti nasion, dagiti nakaskasdaaw nga aramidna kadagiti amin a nasion.
Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
25 Ta naindaklan ni Yahweh ket masapul a mapadayawan unay, ket isuna ti nangnangruna a pagbutngan ngem kadagiti amin a didios.
Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
26 Ta dagiti amin a dios dagiti nasion ket didiosen, ngem ni Yahweh ti namarsua kadagiti langlangit.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
27 Ti kinadayag ken kinatan-ok ket adda iti presensiana. Ti pannakabalin ken rag-o ket adda iti lugarna.
Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
28 Idayawyo ni Yahweh, dakayo a puli dagiti tattao, idayawyo ti dayag ken pigsa ni Yahweh;
Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
29 Idayawyo ni Yahweh iti dayag a maiparbeng iti naganna. Mangyegkayo iti daton ket mapankayo iti sangoananna. Agrukbabkayo kenni Yahweh iti nasantoan a dayagna.
perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
30 Agpigergerkayo iti sangoananna, entero a daga. Naisaad met ti lubong; saan a magunggon.
Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
31 Agraksak koma dagiti langlangit, ken agrag-o koma ti daga; ibagada koma kadagiti nasion, “Agturay ni Yahweh.”
Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
32 Agdaranudor koma ti baybay, ket agpukkaw iti rag-o dagiti adda iti daytoy. Agrag-o koma dagiti tay-ak, ken dagiti amin nga adda kadagitoy.
Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
33 Ket agpukkaw koma gapu iti rag-o dagiti kaykayo iti kabakiran gapu iti rag-o iti sangoanan ni Yahweh, ta umayen isuna a mangukom iti daga.
Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
34 Agyamankayo kenni Yahweh ta naimbag isuna, ta agnanayon ti kinapudnona iti tulagna.
Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 Ket ibagayo, “Isalakannakami, O Dios ti pannakaisalakanmi. Ummongennakami ket ispalennakami manipud kadagiti dadduma a nasion, tapno makapagyamankami iti nasantoan a naganmo ken dayag iti pannakaidayawmo.
Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
36 Madaydayaw koma ni Yahweh a Dios ti Israel iti agnanayon nga awan inggana. Kinuna dagiti amin a tattao, “Amen” ken madaydayaw ni Yahweh.
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
37 Isu nga imbati ni David ni Asaf ken dagiti kakabsatna iti sangoanan ti lakasa ti tulag ni Yahweh, tapno agserbida nga awan sardayna iti sangoanan ti lakasa, kas kasapulan a trabahoen iti inaldaw.
Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
38 Maibilang ni Obed Edom kadagiti innem a pulo ket walo nga agkakabagian. Ni Obed Edom a putot a lalaki ni Jedutun ket kadduana ni Hosa a agbanbantay kadagiti ruangan.
Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
39 Ni Zadok a padi ken dagiti kakadduana a papadi ket agserbida iti sangoanan ti tabernakulo ni Yahweh iti disso a pagdaydayawan idiay Gabaon.
Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
40 Isuda ti kanayon nga agidatag iti altar kadagiti daton a mapuoran para kenni Yahweh, iti agsapa ken rabii, ket surotenda dagiti amin a nakasurat iti linteg ni Yahweh, nga intedna a kas bilin iti Israel.
kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
41 Kadduada da Heman kenni Jedutun, kadduada dagiti dadduma a napili a nainaganan, tapno agyamanda kenni Yahweh, gapu ta agnanayon ti kinapudnona iti tulagna.
Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
42 Da Heman ken Jedutun ti mangimaton kadagiti agpuyot kadagiti tangguyob, dagiti agpiangpiang, ken mangtukar kadagiti dadduma nga instrumento para iti nasagradoan a musika. Dagiti putot a lallaki ni Jedutun ti mangbantay ti ruangan.
Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
43 Ket nagawid dagiti amin a tattao kadagiti pagtaenganda, ken nagawid ni David tapno bendisionanna ti pagtaenganna.
Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

< 1 Cronicas 16 >