< Zsoltárok 45 >
1 Az éneklőmesternek a sosannimra, Kóráh fiainak tanítása; ének a szerelmetesről. Fölbuzog szívem szép beszédre. Mondom: művem a királynak szól. Nyelvem gyors írónak tolla.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Szebb, szebb vagy az ember fiainál, kedvesség ömledez ajakidon, azért áldott meg az Isten örökké.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Kösd derekadra kardodat vitéz! Dicsőségedet és ékességedet.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 És ékességedben haladj diadallal az igazságért, a szelidségért és jogért, és rettenetesre tanítson meg téged a te jobb kezed.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Nyilaid élesek; népek hullanak alád; a király ellenségeinek szívében.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Trónod oh Isten örökkévaló; igazságnak pálczája a te királyságodnak pálczája.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Szereted az igazságot, gyűlölöd a gonoszságot, azért kent fel Isten, a te Istened öröm olajával társaid fölé.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Mirrha, áloe, kácziaillatú minden öltözeted; elefántcsont palotából zeneszóval vidámítnak téged.
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Királyok leányai a te ékességeid; jobb kezed felől királyné áll ofiri aranyban.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Halld csak leány, nézd csak; hajtsd ide füledet! Feledd el népedet és az atyád házát.
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Szépségedet a király kivánja; hiszen urad ő, hódolj hát néki!
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 Tyrus leánya is, a nép dúsai, ajándékkal hizelegnek néked.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Csupa ékesség a király leánya bent, vont aranyból van a ruhája.
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 Hímes öltözetben viszik a királyhoz, szűzek vonulnak utána, az ő társnői; néked hozzák őket.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Bevezetik őket örömmel, vígsággal; bemennek a király palotájába.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Atyáid helyett fiaid lesznek, megteszed őket fejedelmekké mind az egész földön.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Hadd hirdessem a te nevedet nemzedékről nemzedékre; örökkön örökké dicsérnek majd téged a népek!
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.