< Mikeás 7 >
1 Jaj nékem, mert olyanná lettem, mint a letakarított mező, mint a megszedett szőlő: egy enni való gerezd sem maradott; pedig zsengére vágyott a lelkem!
Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
2 Elveszett e földről a kegyes, és igaz sincs az emberek között. Mindnyájan vér után ólálkodnak, kiki hálóval vadássza atyjafiát.
Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
3 Gonoszságra készek a kezek, hogy jól vigyék véghez; a fejedelem követelőzik, és a biró fizetésre vár; a főember is maga mondja el lelke kívánságát, és összeszövik azt.
Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
4 A ki jó közöttök, olyan mint a tüske, az igaz olyan, mint a tövisbokor. A te őrállóidnak napja, a te megítélésed eljött; most következik el az ő zűrzavaruk.
Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
5 Ne higyjetek a barátnak; ne bízzatok a tanácsadóban; az öledben ülő előtt is zárd be szádnak ajtaját.
Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
6 Mert a fiú bolondnak tartja atyját, a leány anyja ellen támad, a meny az ő napára; az embernek saját háznépe az ellensége.
Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
7 De én az Úrra nézek, várom az én szabadításom Istenét; meghallgat engem az én Istenem!
Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
8 Ne örülj, én ellenségem! Elestem ugyan, de felkelek, mert ha még a setétségben ülnék is, az Úr az én világosságom!
Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
9 Az Úr haragját hordozom, mert vétkeztem ellene; mindaddig, a míg leperli peremet és meghozza ítéletemet. Kivisz engem a világosságra, meglátom az ő igazságát.
Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
10 De meglátja ellenségem is és szégyen borítja el, a ki ezt mondja nékem: Hol az Úr, a te Istened? Meglátják őt az én szemeim, hogy ímé széttapostatik, mint az utcza-sár.
Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
11 Falaid megépítésének napja! e napon távol lesz a törvény!
Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
12 Azon a napon eljőnek hozzád Assiriából és Égyiptom városaiból; Égyiptomtól a folyamig, tengertől tengerig és hegytől hegyig.
Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13 És pusztává lesz a föld az ő lakói miatt, az ő cselekedeteik gyümölcséért.
Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
14 Legeltesd népedet a te vessződdel, a te örökségednek nyáját, a mely magánosan lakozik az erdőben, a Kármel közepén. Legeljenek Básánban és Gileádban, mint a hajdankor napjain!
Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
15 Mint az Égyiptom földéről kijövetelednek idején, láttatok vele csodadolgokat.
“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
16 Látják ezt a pogányok és megszégyenülnek minden erejökkel. Kezöket szájokra teszik, füleik megsiketülnek;
Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
17 Nyalják a port, mint a kígyó, mint a föld férgei; reszketve jőnek rejtekeikből; remegve folyamodnak az Úrhoz, a mi Istenünkhöz, és félnek tetőled!
Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
18 Kicsoda olyan Isten, mint te, a ki megbocsátja a bűnt és elengedi öröksége maradékának vétkét?! Nem tartja meg haragját örökké, mert gyönyörködik az irgalmasságban!
Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19 Hozzánk térvén, könyörül rajtunk; eltapodja álnokságainkat. Bizony a tenger mélységébe veted minden bűnünket!
Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20 Hűséget mutatsz a Jákóbnak, irgalmasságot Ábrahámnak, a mint megesküdtél atyáinknak még az ősidőkben.
Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.