< Énekek Éneke 7 >
1 Mily szépek a te lábaid a sarukban, nemesnek leánya te; csipőid fordulatai mint ékszerek, művész kezeinek munkája.
Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
2 Köldököd mint a kerek medencze- ne legyen hiján a kész italnak; hasad buzahalmaz, bekeritve liliomokkal.
Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
3 Két emlőd mint két gida, szarvasünőnek ikrei;
Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
4 nyakad mint elefántcsont-torony, szemeid ama tavak Chesbónban, a népes város kapuja mellett; orrod mint a Libánon tornya, mely Damaszkus felé tekint.
Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
5 Fejed te rajtad mint a Karmel, s fejed hajzata olyan, mint a bíbor: király, megkötve fürtökben.
Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
6 Mily szép vagy és mily kedves vagy, szerelem, a gyönyörüségekben!
Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
7 Ez a te termeted hasonlít a pálmához és emlőid szőlőfürtökhöz;
Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
8 azt mondtam: hadd megyek föl a pálmára, megragadom galyait; s legyenek a te emlőid mint szőlőtőnek fürtjei és orrod illata, mint az almáké,
Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
9 és ínyed mint a jó bor – mely símán folyik barátomnak, megszólaltatja az alvók ajkait.
ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
10 Én barátomé vagyok s hozzám van vágyakozása.
Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
11 Jer, barátom, menjünk ki a mezőre, háljunk meg a falvakon;
Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
12 korán induljunk a szőlőkbe, lássuk, vajon kivirult-e a szőlőtő, megnyílt-e a szőlővirág, kivirágoztak-e a gránátfák: ott adom neked szerelmemet.
Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
13 A nadragulyák illatot adnak és ajtóink mellett mindenféle drága gyümölcsök, újak is, régiek is: számodra, barátom, tettem el.
Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.