< Énekek Éneke 5 >

1 Eljöttem kertembe, én nővérem, én arám, leszedtem myrrhámat fűszeremmel együtt, ettem lépemet a mézemmel együtt, ittam boromat a tejemmel együtt; egyetek, társaim, igyatok és részegedjetek, barátaim!
Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
2 Alszom én, de szívem ébren van. Hallga, barátom kopog: nyiss ki, nővérem, kedvesem, galambom, jámborom, mert fejem harmattal van tele, fürteim az éjnek csepjeivel.
Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 Levetettem köntösömet, hogyan ölteném föl, megmostam lábaimat, hogyan szennyezném be?
Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
4 Barátom benyújtotta kezét a nyíláson, és beleim zúgtak miatta.
Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 Fölkeltem én kinyitni barátomnak, s kezeim cseppegtek myrrhától és ujjaim myrrhától, mely folyt a závár ágaira.
Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
6 Kinyitottam én barátomnak, de barátom elfordult, eltűnt – lelkem elszállt beszéde alatt- kerestem őt, de nem találtam; szólítottam, de nem felelt nekem.
Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 Találtak engem az őrök, kik körüljárnak a városban, vertek engem, megsebesítettek, levették fátyolomat rólam a falak őrei.
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
8 Megesketlek titeket, Jeruzsálem leányai: ha találjátok barátomat, mit mondjatok neki? Hogy betegje vagyok a szerelemnek.
Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
9 Miben különb a barátod más barátnál, te legszebbike az asszonyoknak, miben különb a barátod más barátnál, hogy úgy megesketsz minket?
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
10 Barátom fehér és piros, kiemelkedő tízezer közül;
Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
11 feje finom arany, fürtjei bodrosak, feketék mint a holló;
Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 szemei mint galambok a víz medreinél, tejben fürödnek, foglalatban ülnek;
Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 orczái mint fűszeres virágágyak, illatszereket termők; ajkai liliomok, cseppegve folyó myrrhától;
Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
14 kezei aranyhengerek tarsiskövekkel foglalva, teste remekmű elefántcsontból, borítva zafírkövekkel;
Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
15 lábszárai márványoszlopok, ráillesztve arany talpakra; ábrázata olyan, mint a Libánon, válogatott, mint a czedrusok;
Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 ínye édesség és mindenestől gyönyörűség. Ez az én barátom s ez az én társam, Jeruzsálem leányai!
Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.

< Énekek Éneke 5 >