< Zsoltárok 59 >
1 A karmesternek. Ne ronts szerint. Dávidtól dal. Mikor Sául oda küldött és őrizték a házát, hogy megöljék. Ments meg engem ellenségeimtől, Istenem, támadóimtól ótalmazz engem!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Ments meg a jogtalanságot cselekvőktől, és a vérontás embereitől segíts meg!
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 Mert íme lestek lelkemre, összesereglenek ellenem erősek; se bűntettem, se vétkem nincsen, oh Örökkévaló!
Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 Bűnöm nélkül sürögnek és készülődnek; serkenj elibém és lásd!
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 És te, oh Örökkévaló, Isten, seregek ura, Izraél Istene, ébredj, megbüntetni mind a nemzeteket, ne kegyelmezz mind a jogtalan hűtelenkedőknek! Széla.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 Estére visszatérnek, mordúlnak, mint az eb, s körüljárják a várost.
Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 Íme, szót bugyogtatnak szájukkal, kardok az ajkaikon, mert ki hallja!
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 Te pedig, Örökkévaló, nevetsz, rajtuk, gúnyolódol mind a nemzeteken.
Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 Erőm! Te rád hadd várok, mert Isten a mentsváram.
Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
10 Szeretetem Istene elémbe jön, Isten néznem engedi meglesőimet.
Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Ne öld meg őket, nehogy elfelejtse népem, bujdostasd őket hatalmaddal, és döntsd le őket, oh paizsunk, Uram.
Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 Szájuk vétke, ajkuk szava által fogassanak meg gőgjükben, az esküdözés miatt és hazudozás miatt, melyeket mondogatnak.
Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 Semmísítsd meg hévvel, semmisítsd, hogy ne legyenek; és megtudják, hogy Isten uralkodik Jákóbon a föld végeig. Széla.
muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 S visszatérnek estére, mordúlnak mint az eb, s hörüljárják a vá. rost.
Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Ők bujdosnak eledel után, ha nem laknak jól, úgy kell meghálniok.
Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 Én pedig énekelem erődet, és újjongok reggelre szereteteden; mert mentsvárul voltál nekem s menedékem, a mely napon megszorultam.
Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 Erőm, rólad hadd zengek mert Isten az én mentsváram, szeretetem Istene.
Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.