< Zsoltárok 48 >
1 Ének. Zsoltár Kórach fiaitól. Nagy az Örökkévaló és dicséretes nagyon, Istenünk városában, az ő szent hegyén.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Szép emelkedésű, az egész földnek öröme, Czión hegye — észak hátulján — nagy királynak a vára.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 Kastélyaiban az Isten megismertette magát mentsvárnak.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Mert íme, a királyok összejöttek eltüntek egyetemben.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 Ők láttak, akképen bámultak, megréműltek, elsiettek.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Reszketés fogta el őket ott, vajudás mint a szűlő nőt.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 Keleti széllel összetörsz Tarsís-hajókat.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Ahogy hallottuk, úgy láttuk az Örökkévalónak, a seregek urának városában, Istenünk városában: Isten szilárdítsa azt meg örökre. Széla.
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 Elképzeltük, Isten, a te kegyedet benn a templomodban.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 A milyen a neved Isten, olyan a dicséreted, a föld széléig; igazsággal teli a jobbod.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Örűl Czión hegye, újjonganak Jehúda lányai, ítéleteid okából.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 kerüljétek meg Cziónt, és járjátok körül, számláljátok meg tornyait.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Fordítsátok szíveteket bástyájára, lépdeljetek át kastélyain, azért hogy elbeszéljétek az utóbbi nemzedéknek.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Mert ez Isten, a mi Istenünk, mindörökké; ő vezérel minket holtiglan.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.