< Zsoltárok 45 >

1 A karmesternek. A Liliomok szerint. Kórach fiaitól. Oktató dal. Szerelemnek éneke. Szép beszédre buzdult a szívem; azt mondom én művem a királyé, nyelvem jártas írónak a tolla.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Szépségesebb vagy az ember fiainál, bájosság ömlik el ajkaidon; azért megáldott téged Isten örökre.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Kösd fel kardodat csípődre, oh vitéz, díszedet és ékességedet.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 És ékességedben szökkenj föl, nyargalj az igazság ügyéért és a megalázott jogért, és tanítson téged félelmetes tettekre a te jobbod!
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Nyilaid élesítvék – népek hullanak alád – szívébe a király ellenségeinek.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Trónod, az Istentől való, mindörökké tart, egyenesség pálczája a te királyi pálczád.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Szeretsz igazságot, és gyűlölsz gonoszaágot; azért fölkent téged Isten, a te Istened, vígság olajával a te társaid fölé.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Myrrha és áloé, kasszia mind a ruháid, elefántcsontos palotákból zeneszerekkel örvendeztettek téged.
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Királyok lányai vannak drága nőid közt, ott áll a feleség jobbodon Ófir aranyában.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Halljad leány, lásd és hajlítsd füledet s felejtsd el népedet és atyádnak házát.
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Majd megkivánja a király szépségedet, mert ő az urad, hódolj meg előtte.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 Czór leánya te, ajándékkal hízelegnek neked a népnek gazdagjai.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Merő dicsőség a királyleány ott benn, aranyszövésű az öltözete.
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 Hímzett ruhákban vezetik oda a királynak; hajadonok mögötte, az ő társnői, vitetnek neked.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Oda vezetik őket öröm és újjongás közt, bemennek a király palotájába.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Őseid helyett lesznek majd fiaid, megteszed őket vezérekké az egész országban.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Hadd emlegetem nevedet minden nemzedékben meg nemzedékben; azért magasztalnak téged népek mindörökké.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

< Zsoltárok 45 >