< Példabeszédek 7 >
1 Fiam, őrizd meg mondásaimat és parancsaimat rejtsd el magadnál.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Őrizd meg parancsaimat, hogy élj és tanomat, mint szemeid fényét.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Kösd azokat ujjaidra, írjad azokat szíved táblájára.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Mondd a bölcsességnek: nővérem vagy, s rokonnak nevezd az értelmességet;
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 hogy megőrizzen idegen asszonytól, idegen nőtől, ki simává tette beszédjét.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Mert házam ablakán, rácsozatomon át tekintettem ki.
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 Ekkor láttam az együgyűek között, észre vettem a fiúk közt egy esztelen ifjút:
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 elhalad az utczán annak szöglete mellett és a házához menő úton lépdel,
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 szürkületkor, a nap estéjén, éj sötétségében és homályban.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 S íme elejébe egy asszony, parázna ruhájú és álnok szívű;
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 zajongó ő és csapongó, házában nem nyugosznak lábai:
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 egyszer az utczán, másszor piaczokon, minden szöglet mellett leselkedik.
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Megragadja őt, megcsókolja őt, szemérmetlen arczczal mondja neki:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 Békeáldozatokkal tartozom, ma megfizettem fogadalmaimat;
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 azért jöttem ki elédbe, hogy fölkeressem színedet, és megtaláltalak.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Takarókkal takartam le nyoszolyámat, egyiptomi tarka szövettel;
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 behintettem fekvőhelyemet myrrhával, aloéval s fahéjjal.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Jöjj! ittasodjunk szeretettel reggelig, enyelegjünk szerelemben.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Mert nincs otthon a férfi, útra ment messzire;
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 a pénzes zacskót kezébe vette, holdtölte napjára fog haza jönni.
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Elhajlította őt sok rábeszélésével, ajkai simaságával eltántorítja.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Megy utána hirtelen, mint ökör, mely a levágásra megyen, s mint békóban fenyítéséhez az oktalan;
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 mígnem nyíl fúrja át máját, a mint madár siet a tőrhöz, s nem tudja, hogy életébe kerül.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Most tehát, fiúk, hallgassatok reám s figyeljetek szájam mondásaira:
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 ne térjen az ő utjaira szíved, ne tévelyegj ösvényein;
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 mert sokan vannak a megöltek, kiket elejtett, és számosak mind a meggyilkoltjai.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Az alvilág útjai vannak házában, levisznek a halál kamaráihoz. (Sheol )
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )