< Nehemiás 5 >
1 És nagy volt a népnek s nejeiknek kiáltása zsidó testvéreik ellen.
Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
2 Voltak ugyanis, kik mondták: A mi fiaink és leányaink sokan vannak és vennünk kell gabonát, hogy együnk és éljünk.
Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
3 És voltak, a kik mondták: mezőinket, szőlőinket és házainkat el kell zálogosítanunk, hogy vegyünk gabonát az éhségben.
Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
4 És voltak, a kik mondták: Pénzt vettünk kölcsön a király adójához mezőinkre és szőlőinkre.
Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
5 És most, a milyen testvéreink húsa, olyan a mi húsunk, a milyenek az ő fiaik, olyanok a mi fiaink, s íme kényszerítenünk kell fiainkat a leányainkat szolgákká, és vannak leányaink közül, kik már kényszerítve vannak, nincsen mód a kezünkben, hisz mezőink és szőlőink másokéi.
Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
6 Ez nagyon bosszantott engem, midőn hallottam kiáltásukat és eme beszédeket.
Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
7 És tanácskozott szívem én bennem, és pöröltem a nemesekkel és a vezérekkel és mondtam nekik: Mint hitelezők bántok ti kiki testvérével! És rendeztem ellenük nagy gyülekezetet.
Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
8 És mondtam nekik: Mi megvettük zsidó testvéreinket, a kik eladva voltak a nemzeteknek, a mennyire tőlünk tellett; és ti még el is adnátok testvéreiteket, hogy minekünk eladassanak. Erre hallgattak s nem találtak választ.
ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
9 És mondtam: Nem jó a dolog, a mit ti cselekszetek. Nemde a mi Istenünk félelmében kellene járnotok, a nemzeteknek, ellenségeinknek gyalázása miatt!
Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
10 Én is, meg testvéreim és legényeim az ő hitelezőik vagyunk pénzzel és gabonával, hadd engedjük csak el ezt az adósságot.
Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
11 Adjátok csak vissza nekik e napon mezőiket, szőlőiket, olajfáikat, házaikat és századát a pénznek és a gabonának, mustnak s olajnak, a mivel hitelezőik vagytok.
Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
12 Erre mondták: Visszaadjuk s tőlük mit sem követelünk; úgy cselekszünk, a mint te mondod. És elhívtam a papokat s megeskettem őket, hogy ekképp fognak cselekedni.
Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
13 Ki is ráztam ölemet és mondtam: Így rázzon ki Isten minden embert, a ki ezt a dolgot nem teljesíti, házából és szerzeményéből s így legyen kirázott és üres. Erre mondta az egész gyülekezet: Ámen! És dicsérték az Örökkévalót, és cselekedett a nép ezenképpen.
Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
14 Attól a naptól fogva is, a melyen kirendeltek engem, hogy helytartójuk legyek Jehúda országában, huszadik évétől harminckettedik évéig Artachsaszt királynak, tizenkét éven át, én a testvéreimmel a helytartó kenyerét nem ettem.
Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
15 Az előbbi helytartók pedig, a kik előttem voltak, megterhelték a népet és vettek tőlük kenyér és bor fejében több mint negyven sékel ezüstöt, a legényeik is hatalmaskodtak a nép fölött; de én nem cselekedtem így, istenfélelemből.
Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
16 És e fal munkájában is erősködtem s mezőt nem vettünk, mind a legényeim pedig egybegyűlve voltak ott a munkánál.
Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
17 A zsidók pedig, mind a vezérek, százötven ember, s azok, a kik hozzánk jöttek a körülöttünk levő nemzetek közül, asztalomnál voltak.
Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
18 A mi pedig elkészíttetett egy napra: egy ökör, hat válogatott juh, és szárnyasok készíttettek el nekem és tíz napon belül jó sok mindenféle borból; mindamellett a helytartó kenyerét nem követeltem, mert terhes volt a szolgálat ezen a népen.
Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
19 Emlékezzél meg, Istenem, javamra mindarról, a mit ezért a népért cselekedtem.
Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.