< Mikeás 1 >

1 Az Örökkévaló igéje, mely lett a Mórésetbeli Míkhához Jótám, Ácház, Jechizkíja Jehúda királyainak napjaiban, a mit látott Sómrón és Jeruzsálem felől.
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Halljátok ti népek mind, figyelj föld meg teljessége! És legyen az Úr, az Örökkévaló tanúul ellenetek, az Úr az ő szent templomából.
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
3 Mert íme, az Örökkévaló kivonul helyéről és leszáll és lépdel a föld magaslatain;
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 elolvadnak a hegyek ő alatta és a völgyek széthasadnak, mint a viasz a tűz elől, mint lejtőn leomló vizek.
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 Jákób bűntetteért mind ez, és Izraél házának vétkeiért! Mi Jákób bűntette? Nemde Sómrón! És mik Jehúda magaslata? Nemde Jeruzsálem!
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
6 Teszem tehát Sómrónt rommá a mezőn, szőlőültetvényekké, leomlasztom a völgybe köveit, és alapjait föltárom.
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
7 Mind a faragott képei összetöretnek, s mind az ajándokai tűzben égettetnek el, és mind a bálványait pusztulássá teszem, mert parázna-ajándokból gyűjtötte össze, és ismét parázna-ajándokká vállnak.
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
8 E miatt hadd tartok gyászt s hadd jajgatok, hadd járok mezítláb és meztelenül; teszek oly siralmat, mint a sakálok, gyászt mint a struczmadarak.
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
9 Mert végzetes a csapása, mert eljutott Jehúdáig, odaért népem kapujához, Jeruzsálemhez!
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 Gátban ne jelentsétek, sírni ne sírjatok, Bét-Afrában porban fetrengj!
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
11 Költözzél el, Sáfír lakója, szégyenre meztelenítve! Nem vonult ki Czáanán lakója, Bét-Éczel siralma elveszi tőletek az állomását.
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
12 Mert remegett a jóért Márót lakója, mert baj szállt alá az Örökkévalótól Jeruzsálem kapujára.
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Fogd be a szekérbe az állatot, Lákhís lakója – vétek elseje az Czión leányának- mert benned találtattak Izraél bűntettei.
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
14 Azért hozzá adsz kísérő ajándékot Móréset-Gáthoz; Akhzíb házai csalókává lesznek Izraél királyainak.
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
15 Még hozom reád az elfoglalót, Márésa lakója! Egész Adullámig jutni fog Izraél dicsősége.
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
16 Kopaszd és nyírd magadat gyönyörűséges gyermekeid miatt, tágítsd kopaszságodat mint a sas, mert számkivetésbe mentek tőled.
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

< Mikeás 1 >