< 3 Mózes 13 >
1 És szólt az Örökkévaló Mózeshez meg Áronhoz mondván:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
2 Ha lesz valamely ember testének bőrén daganat, vagy var, vagy világos folt és lehet testének bőrén poklos sérelemmé, akkor vitessék Áronhoz, a paphoz vagy fiai egyikéhez a papok közül.
“Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
3 És nézze meg a pap a sérelmét a test bőrén, ha a szőr a sérelemben átváltozott fehérré, a sérelem színe pedig mélyebb a test bőrénél, poklos sérelem az; amint megnézi a pap, tisztátalannak jelentse ki azt.
Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
4 Ha pedig fehér volt az testének bőrén és színe nem mélyebb a bőrnél és szőre sem változott át fehérré, akkor zárja el a pap a sérelmet hét napra.
Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
5 És nézze meg a pap a hetedik napon és íme a sérelem megmaradt a maga színében, nem terjedt a sérelem a bőrön, akkor zárja el a pap hét napra másodszor.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
6 És megnézi azt a pap a hetedik napon másodszor és íme homályosodott a sérelem, de nem terjedt a sérelem a bőrön, akkor tisztának jelentse ki a pap, var az; mossa meg a ruháit és tiszta lesz.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
7 Ha azonban terjed a var a bőrön, miután megmutatta magát a papnak tisztulás végett, akkor mutassa meg magát másodszor a papnak.
Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
8 És nézze meg a pap és íme, terjedt a var a bőrön, akkor tisztátalannak jelentse ki a pap, poklosság az.
Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
9 Poklos sérelem, ha lesz valamely emberen, vitessék el a paphoz;
“Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
10 nézze meg a pap és íme, fehér daganat van a bőrön és ez átváltoztatta a szőrt fehérré, és vad hús növése van a daganatban,
Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
11 idült poklosság az testének bőrén, tisztátalannak jelentse ki a pap; ne zárja el, mert tisztátalan ő.
limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
12 Ha pedig fölfakad a poklosság a bőrön és elfedi a poklosság a sérelemnek egész bőrét, tetőtől talpig, amennyire látnak a pap szemei,
“Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
13 megnézi a pap és íme, elfödte a poklosság egész testét, akkor tisztának jelentse ki a sérelmet, az egész átváltozott fehérré, tiszta az.
wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
14 De amely napon mutatkozik rajta vad hús, tisztátalan az.
Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
15 És megnézi a pap a vad húst és tisztátalannak jelenti ki a vad hús tisztátalan, poklosság az.
Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
16 Vagy ha a vad hús újra fehérré változik, akkor menjen el a paphoz;
Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
17 és megnézi őt a pap és íme, átváltozott a sérelem fehérré, akkor tisztának jelentse ki a pap a sérelmet, tiszta az.
Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
18 A test, melynek bőrén fekély van és meggyógyul,
“Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
19 de a fekély helyén fehér daganat támad vagy fehérvöröses folt akkor mutassa meg magát a papnak.
ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
20 És megnézi a pap és íme, színe alacsonyabb a bőrnél és szőre átváltozott fehérré, akkor tisztátalannak jelentse ki a pap, poklos sérelem az, a fekélyben fakadt.
Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
21 Ha pedig megnézi a pap és íme, nincs benne fehér szőr és nem is alacsonyabb a bőrnél és homályos az, akkor zárja el a pap hét napra.
Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
22 Ha azonban terjed a bőrön, akkor tisztátalannak jelentse ki a pap, sérelem az.
Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
23 Ha pedig helyén marad a folt, nem terjedt, a fekély hegedése az; tisztának jelentse ki a pap.
Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
24 Vagy ha valamely test bőrén tűzégési seb lesz és támad az égés hegedésében vörösesfehér folt vagy fehér;
“Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
25 és megnézi azt a pap és íme, elváltozott a fehér szőr a folton és színe mélyebb a bőrnél, poklosság az, az égésben fakadt; tisztátalannak jelentse ki őt a pap, poklos sérelem az.
wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
26 Ha azonban megnézi a pap és íme nincs a foltban fehér szőr és nem is alacsonyabb a bőrnél és homályos az, akkor zárja el őt a pap hét napra.
Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
27 Azután megnézi a pap a hetedik napon, ha terjedt a bőrön, tisztátalannak jelentse ki a pap, poklos sérelem az.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
28 Ha pedig megmarad a helyén a folt, nem terjedt a bőrön és homályos, az égési seb daganata az, tisztának jelentse ki a pap, mert az égési seb forradása az.
Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
29 Férfi vagy nő, ha lesz rajta sérelem, a fejen vagy a szakállon,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
30 és megnézi a pap a sérelmet és íme, színe mélyebb a bőrnél és benne aranysárga apró szőr akkor tisztátalannak jelentse ki a pap, ótvar az, poklossága az a fejnek vagy a szakállnak.
wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
31 De ha megnézi a pap az ótvar sérelmét és íme, színe nem mélyebb a bőrnél és fekete szőr sincs benne, akkor zárja el a pap az ótvar sérelmét hét napra.
Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
32 Megnézi a pap a sérelmet a hetedik napon és íme, nem terjedt az ótvar és nem lett benne aranysárga szőr és az ótvarnak színe nem mélyebb a bőrnél,
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
33 akkor nyiratkozzék meg, de az ótvart ne nyírja le; hanem zárja el a pap az ótvart hét napra, másodszor.
wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
34 És megnézi a pap az ótvart a hetedik napon és íme, nem terjedt az ótvar a bőrön és színe sem mélyebb a bőrnél, akkor tisztának jelentse ki, a pap; mossa meg az a ruháit és tiszta lesz.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
35 De ha terjed az ótvar a bőrön, megtisztulása után,
Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
36 és megnézi a pap és íme, terjedt az ótvar a bőrön, akkor ne kutassa a pap az aranysárga szőrt, tisztátalan az.
wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
37 De ha megmarad az ő színében az ótvar és fekete szőr nőtt benne, akkor meggyógyult az ótvar, tiszta az, tisztának jelentse ki a pap.
Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
38 És férfi vagy nő, ha lesznek testük bőrén foltok, fehér foltok,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
39 megnézi a pap és íme, testük bőrén homályos, fehér foltok vannak, fehér var az, a bőrön fakadt, tiszta az.
wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
40 És férfiú, ha kihull fejének haja, kopasz az tiszta az.
“Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
41 Ha pedig arca felől hull ki a haja, elől kopasz az, tiszta az.
Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
42 Ha azonban a kopaszságon vagy elől kopasz fején vörösesfehér sérelem támad, felfakadó poklosság az kopaszságán vagy elől kopasz fején.
Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
43 Megnézi azt a pap és íme, a sérelem daganata vörösesfehér, kopaszságán vagy elől kopasz fején, mint a poklosság színe a test bőrén,
Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
44 poklos férfiú ő, tisztátalan ő; tisztátalannak jelentse ki őt a pap, fején van a sérelme.
ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
45 És a poklos, akin a sérelem van, ruhái legyenek megszaggatva és feje vadul benőve és bajuszáig burkolózzék be és kiáltsa: tisztátalan, tisztátalan.
“Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
46 Mindama napokban, míg a sérelem rajta van, legyen tisztátalan; tisztátalan ő, egyedül lakjék, a táboron kívül legyen lakhelye.
Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
47 És ha valamely ruhán lesz poklos sérelem, gyapjúruhán vagy lenruhán,
“Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
48 akár a mellékfonálon, akár a bélfonálon, lenből vagy gyapjúból, vagy bőrön vagy bármi bőrmunkán,
kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
49 és lesz a sérelem zöldes vagy vöröses a ruhán vagy a bőrön, akár a mellékfonálon, akár a bélfonálon, vagy bármi bőreszközön, poklos sérelem az, mutassák meg a papnak.
ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
50 Nézze meg a pap a sérelmet és zárja el a sérelmet hét napra.
Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
51 És nézze meg a sérelmet a hetedik napon, ha terjedt a sérelem a ruhán, akár a mellékfonálon, akár a bélfonálon, vagy a bőrön, bármely munkán, amivé a bőr feldolgozható, emésztő poklosság a sérelem, tisztátalan az.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
52 És égesse el a ruhát, akár a mellékfonalat, akár a bélfonalat a gyapjúból vagy a lenből, vagy mind a bőreszközt, amelyen lesz a sérelem, mert emésztő poklosság az, tűzben égettessék el.
Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
53 Ha pedig megnézi a pap és íme, nem terjedt a sérelem a ruhán, sem a mellékfonálon, sem a bélfonálon, vagy bármely bőreszközön,
“Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
54 akkor parancsolja meg a pap, hogy mossák meg azt, amin a sérelem van és zárja el hét napra, másodszor.
iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
55 És megnézi a pap, miután megmosták a sérelmet és íme, nem változtatta el a sérelem a színét és nem terjedt a sérelem, tisztátalan az, tűzben égessék el azt; romlás az, visszáján vagy színén.
Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
56 Ha pedig megnézte a pap és íme, homályos a sérelem, miután megmosták azt, akkor tépje ki a ruhából vagy a bőrből, akár a mellékfonálból, akár a bélfonálból.
Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
57 És ha ismét meglátszik a ruhán, akár a mellékfonálon, akár a bélfonálon, vagy bármi bőreszközön, újrafakadó az; tűzben égessék el azt, amin a sérelem van.
Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
58 És a ruhát, akár a mellékfonalat, akár a bélfonalat, vagy bármely bőreszközt, melyet megmoshatsz és távozik belőlük a sérelem, mossák meg másodszor és tiszta lesz.
Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
59 Ez a tana, a poklos sérelemnek a gyapjú vagy lenruhán, akár a mellékfonálon, akár a bélfonálon, vagy bármi bőreszközön, hogy tisztának vagy tisztátalannak jelentsék ki azt.
Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.