< Jób 36 >
1 És folytatta Elíhú és mondta:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Várj reám egy kicsit, hadd közöljem veled, mert még van Isten mellett mondani valóm.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Messzünnen hozom tudásomat és alkotómnak adok igazat.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Mert valóban, szavaim nem hazugság, teljes tudású van szemben veled.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Lám, Isten hatalmas, de kit sem vet meg, észerőre hatalmas.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Nem hagyja életben a gonoszt, s a szegényeknek jogát megadja.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Nem vonja el az igaztól szemeit, sőt királyok mellé, a trónra ültette őket örökre, hogy kimagasodtak.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 S ha bilincsekkel vannak megkötve, ha megfogatnak a nyomorúság köteleivel:
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 megmondja nekik cselekedetüket és bűntetteiket, hogy hősködtek;
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 megnyitja fülüket a feddésnek és azt mondja, hogy térjenek meg a jogtalanságtól.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Ha hallgatnak rá és szolgálják őt, jólétben töltik el végig napjaikat és éveiket kellemetességben;
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 de ha nem hallgatnak reá, fegyver által tűnnek el s kimúlnak megismerés híján.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 S az istentelen szívűek haragot táplálnak, nem esedeznek, midőn megkötözte őket.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Ifjúkorban kell elhalnia lelküknek és életüknek a ledérek között.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Kiszabadítja a nyomorgót nyomorúsága által s a szorongatás által megnyitja fülüket.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Kicsábít téged is a szükség szájából, tág térre, melynek helyén nincs szorongás, s a mi rászáll asztalodra, tele van zsiradékkal.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 De ha a gonosz ítéletével vagy tele, ítélet és törvény megragadnak téged.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Bizony, ne csábítson el téged a harag tömérdekségével és a váltság bősége ne hajlítson el.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Hát szorongás nélkül rendezze-e segítségedet s az erőszak minden megfeszítése nélkül?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Ne áhítsd az éjéjszakát, midőn népek tűnnek el helyükről.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Őrizkedjél, ne fordulj jogtalanság felé, mert ezt inkább választottad a nyomorúságnál.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Lám, Isten felmagasztosul erejében; ki olyan oktató, mint ő!
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Ki kéri számon tőle útját, s ki mondja: jogtalanságot műveltél!
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Gondolj rá, hogy magasztald művét, melyet szemléltek férfiak;
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 mind az emberek néztek rá, a halandó messziről tekinti.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Lám, Isten magasztos, nem ismerjük meg, éveinek száma ki nem kutatható.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Mert felvonja a víznek cseppjeit, hogy az ő köde számára tisztuljanak esővé,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 melyet folyatnak a fellegek, csurgatnak a sok emberre.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Avagy értik-e a felhő terjedelmeit, sátrának robaját?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Lám, magára terítette fényét s ráborította a tenger gyökereit,
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 mert velök ítél népeket, eleséget ád busásan.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Kezeire fényt borított s kirendelte azt a támadó ellen.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Hirdet róla az ő dörgése, a csorda is a keletkező viharról.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.