< भजन संहिता 129 >

1 यात्रा का गीत इस्राएल अब यह कहे, “मेरे बचपन से लोग मुझे बार बार क्लेश देते आए हैं,
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 मेरे बचपन से वे मुझ को बार बार क्लेश देते तो आए हैं, परन्तु मुझ पर प्रबल नहीं हुए।
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 हलवाहों ने मेरी पीठ के ऊपर हल चलाया, और लम्बी-लम्बी रेखाएँ की।”
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 यहोवा धर्मी है; उसने दुष्टों के फंदों को काट डाला है;
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 जितने सिय्योन से बैर रखते हैं, वे सब लज्जित हों, और पराजित होकर पीछे हट जाए!
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 वे छत पर की घास के समान हों, जो बढ़ने से पहले सूख जाती है;
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 जिससे कोई लवनेवाला अपनी मुट्ठी नहीं भरता, न पूलियों का कोई बाँधनेवाला अपनी अँकवार भर पाता है,
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 और न आने-जानेवाले यह कहते हैं, “यहोवा की आशीष तुम पर होवे! हम तुम को यहोवा के नाम से आशीर्वाद देते हैं!”
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

< भजन संहिता 129 >