< विलापगीत 3 >
1 मैं वह व्यक्ति हूं, जिसने याहवेह के कोप-दण्ड में पीड़ा का साक्षात अनुभव किया है.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 उन्होंने हकालते हुए मुझे घोर अंधकार में डाल दिया है कहीं थोड़ा भी प्रकाश दिखाई नहीं देता;
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 निश्चयतः बार-बार, सारे दिन उनका कठोर हाथ मेरे विरुद्ध सक्रिय बना रहता है.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 मेरा मांस तथा मेरी त्वचा गलते जा रहे हैं और उन्होंने मेरी अस्थियों को तोड़ दिया है.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 उन्होंने मुझे पकड़कर कष्ट एवं कड़वाहट में लपेट डाला है.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 उन्होंने मुझे इस प्रकार अंधकार में रहने के लिए छोड़ दिया है मानो मैं दीर्घ काल से मृत हूं.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 उन्होंने मेरे आस-पास दीवार खड़ी कर दी है, कि मैं बचकर पलायन न कर सकूं; उन्होंने मुझे भारी बेड़ियों में बांध रखा है.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 मैं सहायता की दोहाई अवश्य देता हूं, किंतु वह मेरी पुकार को अवरुद्ध कर देते हैं.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 उन्होंने मेरे मार्गों को पत्थर लगाकर बाधित कर दिया है; उन्होंने मेरे मार्गों को विकृत बना दिया है.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 वह एक ऐसा रीछ है, ऐसा सिंह है, जो मेरे लिए घात लगाए हुए बैठा है,
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 मुझे भटका कर मुझे टुकड़े-टुकड़े कर डाला और उसने मुझे निस्सहाय बना छोड़ा है.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 उन्होंने अपना धनुष चढ़ाया तथा मुझे अपने बाणों का लक्ष्य बना लिया.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 अपने तरकश से बाण लेकर उन्होंने उन बाणों से मेरा हृदय बेध दिया.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 सभी के लिए अब तो मैं उपहास पात्र हूं; सारे दिन उनके व्यंग्य-बाण मुझ पर छोड़े जाते हैं.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 उन्होंने मुझे कड़वाहट से भर दिया है उन्होंने मुझे नागदौने से सन्तृप्त कर रखा है.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 उन्होंने मुझे कंकड़ों पर दांत चलाने के लिए विवश कर दिया है; मुझे भस्म के ढेर में जा छिपने के लिए विवश कर दिया है.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 शांति ने मेरी आत्मा का साथ छोड़ दिया है; मुझे तो स्मरण ही नहीं रहा कि सुख-आनन्द क्या होता है.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 इसलिये मुझे यही कहना पड़ रहा है, “न मुझमें धैर्य शेष रहा है और न ही याहवेह से कोई आशा.”
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 स्मरण कीजिए मेरी पीड़ा और मेरी भटकन, वह नागदौन तथा वह कड़वाहट.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 मेरी आत्मा को इसका स्मरण आता रहता है, मेरा मनोबल शून्य हुआ जा रहा है.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 मेरी आशा मात्र इस स्मृति के आधार पर जीवित है:
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 याहवेह का करुणा-प्रेम, के ही कारण हम भस्म नही होते! कभी भी उनकी कृपा का ह्रास नहीं होता.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 प्रति प्रातः वे नए पाए जाते हैं; महान है आपकी विश्वासयोग्यता.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 मेरी आत्मा इस तथ्य की पुष्टि करती है, “याहवेह मेरा अंश हैं; इसलिये उनमें मेरी आशा रखूंगा.”
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 याहवेह के प्रिय पात्र वे हैं, जो उनके आश्रित हैं, वे, जो उनके खोजी हैं;
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 उपयुक्त यही होता है कि हम धीरतापूर्वक याहवेह द्वारा उद्धार की प्रतीक्षा करें.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 मनुष्य के लिए हितकर यही है कि वह आरंभ ही से अपना जूआ उठाए.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 वह एकाकी हो शांतिपूर्वक इसे स्वीकार कर ले, जब कभी यह उस पर आ पड़ता है.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 वह अपना मुख धूलि पर ही रहने दे— आशा कभी मृत नहीं होती.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 वह अपना गाल उसे प्रस्तुत कर दे, जो उस प्रहार के लिए तैयार है, वह समस्त अपमान स्वीकार कर ले.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 प्रभु का परित्याग चिरस्थायी नहीं हुआ करता.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 यद्यपि वह पीड़ा के कारण तो हो जाते हैं, किंतु करुणा का सागर भी तो वही हैं, क्योंकि अथाह होता है उनका करुणा-प्रेम.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 पीड़ा देना उनका सुख नहीं होता न ही मनुष्यों को यातना देना उनका आनंद होता है.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 पृथ्वी के समस्त बंदियों का दमन,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 परम प्रधान की उपस्थिति में न्याय-वंचना,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 किसी की न्याय-दोहाई में की गई विकृति में याहवेह का समर्थन कदापि नहीं होता?
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 यदि स्वयं प्रभु ने कोई घोषणा न की हो, तो किसमें यह सामर्थ्य है, कि जो कुछ उसने कहा है, वह पूरा होगा?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 क्या यह तथ्य नहीं कि अनुकूल अथवा प्रतिकूल, जो कुछ घटित होता है, वह परम प्रधान के बोलने के द्वारा ही होता है?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 भला कोई जीवित मनुष्य अपने पापों के दंड के लिए परिवाद कैसे कर सकता है?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 आइए हम अपनी नीतियों का परीक्षण करें तथा अपने याहवेह की ओर लौट चलें:
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 आइए हम अपने हृदय एवं अपनी बांहें परमेश्वर की ओर उन्मुख करें तथा अपने हाथ स्वर्गिक परमेश्वर की ओर उठाएं:
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 “हमने अपराध किए हैं, हम विद्रोही हैं, आपने हमें क्षमा प्रदान नहीं की है.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 “आपने स्वयं को कोप में भरकर हमारा पीछा किया; निर्दयतापूर्वक हत्यायें की हैं.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 आपने स्वयं को एक मेघ में लपेट रखा है, कि कोई भी प्रार्थना इससे होकर आप तक न पहुंच सके.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 आपने हमें राष्ट्रों के मध्य कीट तथा कूड़ा बना छोड़ा है.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 “हमारे सभी शत्रु बेझिझक हमारे विरुद्ध निंदा के शब्द उच्चार रहे हैं.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 आतंक, जोखिम, विनाश तथा विध्वंस हम पर आ पड़े हैं.”
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 मेरी प्रजा के इस विनाश के कारण मेरे नेत्रों के अश्रुप्रवाह नदी सदृश हो गए हैं.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 बिना किसी विश्रान्ति मेरा अश्रुपात होता रहेगा,
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 जब तक स्वर्ग से याहवेह इस ओर दृष्टिपात न करेंगे.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 अपनी नगरी की समस्त पुत्रियों की नियति ने मेरे नेत्रों को पीड़ित कर रखा है.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 उन्होंने, जो अकारण ही मेरे शत्रु हो गए थे, पक्षी सदृश मेरा अहेर किया है.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 उन्होंने तो मुझे गड्ढे में झोंक मुझ पर पत्थर लुढ़का दिए हैं;
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 जब जल सतह मेरे सिर तक पहुंचने लगी, मैं विचार करने लगा, अब मैं मिट जाऊंगा.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 गड्ढे से मैंने, याहवेह आपकी दोहाई दी.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 आपने मेरी इस दोहाई सुन ली है: “मेरी विमुक्ति के लिए की गई मेरी पुकार की ओर से, अपने कान बंद न कीजिए.”
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 जब मैंने आपकी दोहाई दी, आप निकट आ गए; आपने आश्वासन दिया, “डरो मत.”
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 प्रभु आपने मेरा पक्ष लेकर; मेरे जीवन को सुरक्षा प्रदान की है.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 याहवेह, आपने वह अन्याय देख लिया है, जो मेरे साथ किया गया है. अब आप मेरा न्याय कीजिए!
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 उनके द्वारा लिया गया बदला आपकी दृष्टि में है, उनके द्वारा रचे गए सभी षड़्यंत्र आपको ज्ञात हैं.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 याहवेह, आपने उनके द्वारा किए गए व्यंग्य सुने हैं, उनके द्वारा रचे गए सभी षड़्यंत्र आपको ज्ञात हैं—
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 मेरे हत्यारों के हृदय में सारे दिन जो विचार उभरते हैं होंठों से निकलते हैं, मेरे विरुद्ध ही होते हैं.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 आप ही देख लीजिए, उनका उठना-बैठना, मैं ही हूं उनका व्यंग्य-गीत.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 याहवेह, उनके कृत्यों के अनुसार, उन्हें प्रतिफल तो आप ही देंगे.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 आप उनके हृदय पर आवरण डाल देंगे, उन पर आपका शाप प्रभावी हो जाएगा!
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 याहवेह, आप अपने स्वर्गलोक से उनका पीछा कर उन्हें नष्ट कर देंगे.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.