< תהילים 7 >

שגיון לדוד אשר שר ליהוה על דברי כוש בן ימיני יהוה אלהי בך חסיתי הושיעני מכל רדפי והצילני׃ 1
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
פן יטרף כאריה נפשי פרק ואין מציל׃ 2
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
יהוה אלהי אם עשיתי זאת אם יש עול בכפי׃ 3
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
אם גמלתי שולמי רע ואחלצה צוררי ריקם׃ 4
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
ירדף אויב נפשי וישג וירמס לארץ חיי וכבודי לעפר ישכן סלה׃ 5
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
קומה יהוה באפך הנשא בעברות צוררי ועורה אלי משפט צוית׃ 6
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
ועדת לאמים תסובבך ועליה למרום שובה׃ 7
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
יהוה ידין עמים שפטני יהוה כצדקי וכתמי עלי׃ 8
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
יגמר נא רע רשעים ותכונן צדיק ובחן לבות וכליות אלהים צדיק׃ 9
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
מגני על אלהים מושיע ישרי לב׃ 10
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
אלהים שופט צדיק ואל זעם בכל יום׃ 11
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
אם לא ישוב חרבו ילטוש קשתו דרך ויכוננה׃ 12
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
ולו הכין כלי מות חציו לדלקים יפעל׃ 13
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
הנה יחבל און והרה עמל וילד שקר׃ 14
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
בור כרה ויחפרהו ויפל בשחת יפעל׃ 15
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
ישוב עמלו בראשו ועל קדקדו חמסו ירד׃ 16
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
אודה יהוה כצדקו ואזמרה שם יהוה עליון׃ 17
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

< תהילים 7 >