< תהילים 48 >
שיר מזמור לבני קרח גדול יהוה ומהלל מאד בעיר אלהינו הר קדשו׃ | 1 |
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
יפה נוף משוש כל הארץ הר ציון ירכתי צפון קרית מלך רב׃ | 2 |
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
אלהים בארמנותיה נודע למשגב׃ | 3 |
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
כי הנה המלכים נועדו עברו יחדו׃ | 4 |
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
המה ראו כן תמהו נבהלו נחפזו׃ | 5 |
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
רעדה אחזתם שם חיל כיולדה׃ | 6 |
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
ברוח קדים תשבר אניות תרשיש׃ | 7 |
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
כאשר שמענו כן ראינו בעיר יהוה צבאות בעיר אלהינו אלהים יכוננה עד עולם סלה׃ | 8 |
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
דמינו אלהים חסדך בקרב היכלך׃ | 9 |
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
כשמך אלהים כן תהלתך על קצוי ארץ צדק מלאה ימינך׃ | 10 |
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
ישמח הר ציון תגלנה בנות יהודה למען משפטיך׃ | 11 |
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
סבו ציון והקיפוה ספרו מגדליה׃ | 12 |
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
שיתו לבכם לחילה פסגו ארמנותיה למען תספרו לדור אחרון׃ | 13 |
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
כי זה אלהים אלהינו עולם ועד הוא ינהגנו על מות׃ | 14 |
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.