< תהילים 46 >

למנצח לבני קרח על עלמות שיר אלהים לנו מחסה ועז עזרה בצרות נמצא מאד׃ 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali. Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.
על כן לא נירא בהמיר ארץ ובמוט הרים בלב ימים׃ 2
Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike, ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,
יהמו יחמרו מימיו ירעשו הרים בגאותו סלה׃ 3
ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu, ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.
נהר פלגיו ישמחו עיר אלהים קדש משכני עליון׃ 4
Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu, malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.
אלהים בקרבה בל תמוט יעזרה אלהים לפנות בקר׃ 5
Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa; Mulungu adzawuthandiza mmawa.
המו גוים מטו ממלכות נתן בקולו תמוג ארץ׃ 6
Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa; Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.
יהוה צבאות עמנו משגב לנו אלהי יעקב סלה׃ 7
Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
לכו חזו מפעלות יהוה אשר שם שמות בארץ׃ 8
Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova, chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.
משבית מלחמות עד קצה הארץ קשת ישבר וקצץ חנית עגלות ישרף באש׃ 9
Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi; Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo; amatentha zishango ndi moto.
הרפו ודעו כי אנכי אלהים ארום בגוים ארום בארץ׃ 10
Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu; ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu; ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”
יהוה צבאות עמנו משגב לנו אלהי יעקב סלה׃ 11
Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

< תהילים 46 >