< תהילים 37 >
לדוד אל תתחר במרעים אל תקנא בעשי עולה׃ | 1 |
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
כי כחציר מהרה ימלו וכירק דשא יבולון׃ | 2 |
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
בטח ביהוה ועשה טוב שכן ארץ ורעה אמונה׃ | 3 |
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
והתענג על יהוה ויתן לך משאלת לבך׃ | 4 |
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
גול על יהוה דרכך ובטח עליו והוא יעשה׃ | 5 |
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
והוציא כאור צדקך ומשפטך כצהרים׃ | 6 |
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
דום ליהוה והתחולל לו אל תתחר במצליח דרכו באיש עשה מזמות׃ | 7 |
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
הרף מאף ועזב חמה אל תתחר אך להרע׃ | 8 |
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
כי מרעים יכרתון וקוי יהוה המה יירשו ארץ׃ | 9 |
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
ועוד מעט ואין רשע והתבוננת על מקומו ואיננו׃ | 10 |
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
וענוים יירשו ארץ והתענגו על רב שלום׃ | 11 |
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
זמם רשע לצדיק וחרק עליו שניו׃ | 12 |
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
אדני ישחק לו כי ראה כי יבא יומו׃ | 13 |
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
חרב פתחו רשעים ודרכו קשתם להפיל עני ואביון לטבוח ישרי דרך׃ | 14 |
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
חרבם תבוא בלבם וקשתותם תשברנה׃ | 15 |
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
טוב מעט לצדיק מהמון רשעים רבים׃ | 16 |
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
כי זרועות רשעים תשברנה וסומך צדיקים יהוה׃ | 17 |
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
יודע יהוה ימי תמימם ונחלתם לעולם תהיה׃ | 18 |
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
לא יבשו בעת רעה ובימי רעבון ישבעו׃ | 19 |
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
כי רשעים יאבדו ואיבי יהוה כיקר כרים כלו בעשן כלו׃ | 20 |
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
לוה רשע ולא ישלם וצדיק חונן ונותן׃ | 21 |
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
כי מברכיו יירשו ארץ ומקלליו יכרתו׃ | 22 |
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
מיהוה מצעדי גבר כוננו ודרכו יחפץ׃ | 23 |
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
כי יפל לא יוטל כי יהוה סומך ידו׃ | 24 |
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
נער הייתי גם זקנתי ולא ראיתי צדיק נעזב וזרעו מבקש לחם׃ | 25 |
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
כל היום חונן ומלוה וזרעו לברכה׃ | 26 |
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
סור מרע ועשה טוב ושכן לעולם׃ | 27 |
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
כי יהוה אהב משפט ולא יעזב את חסידיו לעולם נשמרו וזרע רשעים נכרת׃ | 28 |
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
צדיקים יירשו ארץ וישכנו לעד עליה׃ | 29 |
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
פי צדיק יהגה חכמה ולשונו תדבר משפט׃ | 30 |
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
תורת אלהיו בלבו לא תמעד אשריו׃ | 31 |
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
צופה רשע לצדיק ומבקש להמיתו׃ | 32 |
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
יהוה לא יעזבנו בידו ולא ירשיענו בהשפטו׃ | 33 |
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
קוה אל יהוה ושמר דרכו וירוממך לרשת ארץ בהכרת רשעים תראה׃ | 34 |
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
ראיתי רשע עריץ ומתערה כאזרח רענן׃ | 35 |
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
ויעבר והנה איננו ואבקשהו ולא נמצא׃ | 36 |
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
שמר תם וראה ישר כי אחרית לאיש שלום׃ | 37 |
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
ופשעים נשמדו יחדו אחרית רשעים נכרתה׃ | 38 |
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
ותשועת צדיקים מיהוה מעוזם בעת צרה׃ | 39 |
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
ויעזרם יהוה ויפלטם יפלטם מרשעים ויושיעם כי חסו בו׃ | 40 |
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.