< תהילים 29 >
מזמור לדוד הבו ליהוה בני אלים הבו ליהוה כבוד ועז׃ | 1 |
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
הבו ליהוה כבוד שמו השתחוו ליהוה בהדרת קדש׃ | 2 |
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
קול יהוה על המים אל הכבוד הרעים יהוה על מים רבים׃ | 3 |
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
קול יהוה בכח קול יהוה בהדר׃ | 4 |
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
קול יהוה שבר ארזים וישבר יהוה את ארזי הלבנון׃ | 5 |
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
וירקידם כמו עגל לבנון ושרין כמו בן ראמים׃ | 6 |
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
קול יהוה יחיל מדבר יחיל יהוה מדבר קדש׃ | 8 |
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
קול יהוה יחולל אילות ויחשף יערות ובהיכלו כלו אמר כבוד׃ | 9 |
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
יהוה למבול ישב וישב יהוה מלך לעולם׃ | 10 |
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
יהוה עז לעמו יתן יהוה יברך את עמו בשלום׃ | 11 |
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.