< תהילים 139 >
למנצח לדוד מזמור יהוה חקרתני ותדע׃ | 1 |
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
אתה ידעת שבתי וקומי בנתה לרעי מרחוק׃ | 2 |
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
ארחי ורבעי זרית וכל דרכי הסכנתה׃ | 3 |
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
כי אין מלה בלשוני הן יהוה ידעת כלה׃ | 4 |
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
אחור וקדם צרתני ותשת עלי כפכה׃ | 5 |
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
פלאיה דעת ממני נשגבה לא אוכל לה׃ | 6 |
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
אנה אלך מרוחך ואנה מפניך אברח׃ | 7 |
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
אם אסק שמים שם אתה ואציעה שאול הנך׃ (Sheol ) | 8 |
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
אשא כנפי שחר אשכנה באחרית ים׃ | 9 |
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
גם שם ידך תנחני ותאחזני ימינך׃ | 10 |
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
ואמר אך חשך ישופני ולילה אור בעדני׃ | 11 |
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
גם חשך לא יחשיך ממך ולילה כיום יאיר כחשיכה כאורה׃ | 12 |
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
כי אתה קנית כליתי תסכני בבטן אמי׃ | 13 |
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
אודך על כי נוראות נפליתי נפלאים מעשיך ונפשי ידעת מאד׃ | 14 |
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
לא נכחד עצמי ממך אשר עשיתי בסתר רקמתי בתחתיות ארץ׃ | 15 |
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
גלמי ראו עיניך ועל ספרך כלם יכתבו ימים יצרו ולא אחד בהם׃ | 16 |
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
ולי מה יקרו רעיך אל מה עצמו ראשיהם׃ | 17 |
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
אספרם מחול ירבון הקיצתי ועודי עמך׃ | 18 |
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
אם תקטל אלוה רשע ואנשי דמים סורו מני׃ | 19 |
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
אשר יאמרך למזמה נשא לשוא עריך׃ | 20 |
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
הלוא משנאיך יהוה אשנא ובתקוממיך אתקוטט׃ | 21 |
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
תכלית שנאה שנאתים לאויבים היו לי׃ | 22 |
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
חקרני אל ודע לבבי בחנני ודע שרעפי׃ | 23 |
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
וראה אם דרך עצב בי ונחני בדרך עולם׃ | 24 |
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.