< תהילים 137 >

על נהרות בבל שם ישבנו גם בכינו בזכרנו את ציון׃ 1
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
על ערבים בתוכה תלינו כנרותינו׃ 2
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
כי שם שאלונו שובינו דברי שיר ותוללינו שמחה שירו לנו משיר ציון׃ 3
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
איך נשיר את שיר יהוה על אדמת נכר׃ 4
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
אם אשכחך ירושלם תשכח ימיני׃ 5
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
תדבק לשוני לחכי אם לא אזכרכי אם לא אעלה את ירושלם על ראש שמחתי׃ 6
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
זכר יהוה לבני אדום את יום ירושלם האמרים ערו ערו עד היסוד בה׃ 7
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
בת בבל השדודה אשרי שישלם לך את גמולך שגמלת לנו׃ 8
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
אשרי שיאחז ונפץ את עלליך אל הסלע׃ 9
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< תהילים 137 >