< תהילים 122 >
שיר המעלות לדוד שמחתי באמרים לי בית יהוה נלך׃ | 1 |
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
עמדות היו רגלינו בשעריך ירושלם׃ | 2 |
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
ירושלם הבנויה כעיר שחברה לה יחדו׃ | 3 |
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
ששם עלו שבטים שבטי יה עדות לישראל להדות לשם יהוה׃ | 4 |
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
כי שמה ישבו כסאות למשפט כסאות לבית דויד׃ | 5 |
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
שאלו שלום ירושלם ישליו אהביך׃ | 6 |
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
יהי שלום בחילך שלוה בארמנותיך׃ | 7 |
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
למען אחי ורעי אדברה נא שלום בך׃ | 8 |
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
למען בית יהוה אלהינו אבקשה טוב לך׃ | 9 |
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.