< תהילים 116 >
אהבתי כי ישמע יהוה את קולי תחנוני׃ | 1 |
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
כי הטה אזנו לי ובימי אקרא׃ | 2 |
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
אפפוני חבלי מות ומצרי שאול מצאוני צרה ויגון אמצא׃ (Sheol ) | 3 |
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
ובשם יהוה אקרא אנה יהוה מלטה נפשי׃ | 4 |
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
חנון יהוה וצדיק ואלהינו מרחם׃ | 5 |
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
שמר פתאים יהוה דלותי ולי יהושיע׃ | 6 |
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
שובי נפשי למנוחיכי כי יהוה גמל עליכי׃ | 7 |
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
כי חלצת נפשי ממות את עיני מן דמעה את רגלי מדחי׃ | 8 |
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
אתהלך לפני יהוה בארצות החיים׃ | 9 |
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
האמנתי כי אדבר אני עניתי מאד׃ | 10 |
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
אני אמרתי בחפזי כל האדם כזב׃ | 11 |
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
מה אשיב ליהוה כל תגמולוהי עלי׃ | 12 |
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
כוס ישועות אשא ובשם יהוה אקרא׃ | 13 |
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
נדרי ליהוה אשלם נגדה נא לכל עמו׃ | 14 |
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
יקר בעיני יהוה המותה לחסידיו׃ | 15 |
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
אנה יהוה כי אני עבדך אני עבדך בן אמתך פתחת למוסרי׃ | 16 |
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
לך אזבח זבח תודה ובשם יהוה אקרא׃ | 17 |
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
נדרי ליהוה אשלם נגדה נא לכל עמו׃ | 18 |
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
בחצרות בית יהוה בתוככי ירושלם הללו יה׃ | 19 |
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.