< תהילים 111 >

הללו יה אודה יהוה בכל לבב בסוד ישרים ועדה׃ 1
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
גדלים מעשי יהוה דרושים לכל חפציהם׃ 2
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
הוד והדר פעלו וצדקתו עמדת לעד׃ 3
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
זכר עשה לנפלאתיו חנון ורחום יהוה׃ 4
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
טרף נתן ליראיו יזכר לעולם בריתו׃ 5
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
כח מעשיו הגיד לעמו לתת להם נחלת גוים׃ 6
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
מעשי ידיו אמת ומשפט נאמנים כל פקודיו׃ 7
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
סמוכים לעד לעולם עשוים באמת וישר׃ 8
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
פדות שלח לעמו צוה לעולם בריתו קדוש ונורא שמו׃ 9
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
ראשית חכמה יראת יהוה שכל טוב לכל עשיהם תהלתו עמדת לעד׃ 10
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< תהילים 111 >