< תהילים 111 >
הללו יה אודה יהוה בכל לבב בסוד ישרים ועדה׃ | 1 |
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
גדלים מעשי יהוה דרושים לכל חפציהם׃ | 2 |
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
הוד והדר פעלו וצדקתו עמדת לעד׃ | 3 |
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
זכר עשה לנפלאתיו חנון ורחום יהוה׃ | 4 |
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
טרף נתן ליראיו יזכר לעולם בריתו׃ | 5 |
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
כח מעשיו הגיד לעמו לתת להם נחלת גוים׃ | 6 |
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
מעשי ידיו אמת ומשפט נאמנים כל פקודיו׃ | 7 |
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
סמוכים לעד לעולם עשוים באמת וישר׃ | 8 |
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
פדות שלח לעמו צוה לעולם בריתו קדוש ונורא שמו׃ | 9 |
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
ראשית חכמה יראת יהוה שכל טוב לכל עשיהם תהלתו עמדת לעד׃ | 10 |
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.