< תהילים 109 >

למנצח לדוד מזמור אלהי תהלתי אל תחרש׃ 1
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
כי פי רשע ופי מרמה עלי פתחו דברו אתי לשון שקר׃ 2
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
ודברי שנאה סבבוני וילחמוני חנם׃ 3
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
תחת אהבתי ישטנוני ואני תפלה׃ 4
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
וישימו עלי רעה תחת טובה ושנאה תחת אהבתי׃ 5
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
הפקד עליו רשע ושטן יעמד על ימינו׃ 6
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
בהשפטו יצא רשע ותפלתו תהיה לחטאה׃ 7
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
יהיו ימיו מעטים פקדתו יקח אחר׃ 8
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
יהיו בניו יתומים ואשתו אלמנה׃ 9
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
ונוע ינועו בניו ושאלו ודרשו מחרבותיהם׃ 10
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
ינקש נושה לכל אשר לו ויבזו זרים יגיעו׃ 11
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
אל יהי לו משך חסד ואל יהי חונן ליתומיו׃ 12
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
יהי אחריתו להכרית בדור אחר ימח שמם׃ 13
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
יזכר עון אבתיו אל יהוה וחטאת אמו אל תמח׃ 14
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
יהיו נגד יהוה תמיד ויכרת מארץ זכרם׃ 15
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
יען אשר לא זכר עשות חסד וירדף איש עני ואביון ונכאה לבב למותת׃ 16
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
ויאהב קללה ותבואהו ולא חפץ בברכה ותרחק ממנו׃ 17
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
וילבש קללה כמדו ותבא כמים בקרבו וכשמן בעצמותיו׃ 18
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
תהי לו כבגד יעטה ולמזח תמיד יחגרה׃ 19
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
זאת פעלת שטני מאת יהוה והדברים רע על נפשי׃ 20
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
ואתה יהוה אדני עשה אתי למען שמך כי טוב חסדך הצילני׃ 21
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
כי עני ואביון אנכי ולבי חלל בקרבי׃ 22
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
כצל כנטותו נהלכתי ננערתי כארבה׃ 23
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
ברכי כשלו מצום ובשרי כחש משמן׃ 24
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
ואני הייתי חרפה להם יראוני יניעון ראשם׃ 25
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
עזרני יהוה אלהי הושיעני כחסדך׃ 26
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
וידעו כי ידך זאת אתה יהוה עשיתה׃ 27
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
יקללו המה ואתה תברך קמו ויבשו ועבדך ישמח׃ 28
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
ילבשו שוטני כלמה ויעטו כמעיל בשתם׃ 29
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
אודה יהוה מאד בפי ובתוך רבים אהללנו׃ 30
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
כי יעמד לימין אביון להושיע משפטי נפשו׃ 31
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< תהילים 109 >