< מִשְׁלֵי 9 >

חכמות בנתה ביתה חצבה עמודיה שבעה׃ 1
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
טבחה טבחה מסכה יינה אף ערכה שלחנה׃ 2
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
שלחה נערתיה תקרא על גפי מרמי קרת׃ 3
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
מי פתי יסר הנה חסר לב אמרה לו׃ 4
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
לכו לחמו בלחמי ושתו ביין מסכתי׃ 5
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
עזבו פתאים וחיו ואשרו בדרך בינה׃ 6
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
יסר לץ לקח לו קלון ומוכיח לרשע מומו׃ 7
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
אל תוכח לץ פן ישנאך הוכח לחכם ויאהבך׃ 8
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
תן לחכם ויחכם עוד הודע לצדיק ויוסף לקח׃ 9
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
תחלת חכמה יראת יהוה ודעת קדשים בינה׃ 10
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
כי בי ירבו ימיך ויוסיפו לך שנות חיים׃ 11
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
אם חכמת חכמת לך ולצת לבדך תשא׃ 12
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
אשת כסילות המיה פתיות ובל ידעה מה׃ 13
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
וישבה לפתח ביתה על כסא מרמי קרת׃ 14
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
לקרא לעברי דרך המישרים ארחותם׃ 15
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
מי פתי יסר הנה וחסר לב ואמרה לו׃ 16
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
מים גנובים ימתקו ולחם סתרים ינעם׃ 17
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
ולא ידע כי רפאים שם בעמקי שאול קראיה׃ (Sheol h7585) 18
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)

< מִשְׁלֵי 9 >