< מִשְׁלֵי 17 >

טוב פת חרבה ושלוה בה מבית מלא זבחי ריב׃ 1
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
עבד משכיל ימשל בבן מביש ובתוך אחים יחלק נחלה׃ 2
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
מצרף לכסף וכור לזהב ובחן לבות יהוה׃ 3
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
מרע מקשיב על שפת און שקר מזין על לשון הות׃ 4
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
לעג לרש חרף עשהו שמח לאיד לא ינקה׃ 5
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
עטרת זקנים בני בנים ותפארת בנים אבותם׃ 6
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
לא נאוה לנבל שפת יתר אף כי לנדיב שפת שקר׃ 7
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
אבן חן השחד בעיני בעליו אל כל אשר יפנה ישכיל׃ 8
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
מכסה פשע מבקש אהבה ושנה בדבר מפריד אלוף׃ 9
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
תחת גערה במבין מהכות כסיל מאה׃ 10
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
אך מרי יבקש רע ומלאך אכזרי ישלח בו׃ 11
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
פגוש דב שכול באיש ואל כסיל באולתו׃ 12
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
משיב רעה תחת טובה לא תמיש רעה מביתו׃ 13
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
פוטר מים ראשית מדון ולפני התגלע הריב נטוש׃ 14
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
מצדיק רשע ומרשיע צדיק תועבת יהוה גם שניהם׃ 15
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
למה זה מחיר ביד כסיל לקנות חכמה ולב אין׃ 16
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
בכל עת אהב הרע ואח לצרה יולד׃ 17
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
אדם חסר לב תוקע כף ערב ערבה לפני רעהו׃ 18
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
אהב פשע אהב מצה מגביה פתחו מבקש שבר׃ 19
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
עקש לב לא ימצא טוב ונהפך בלשונו יפול ברעה׃ 20
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
ילד כסיל לתוגה לו ולא ישמח אבי נבל׃ 21
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
לב שמח ייטב גהה ורוח נכאה תיבש גרם׃ 22
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
שחד מחיק רשע יקח להטות ארחות משפט׃ 23
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
את פני מבין חכמה ועיני כסיל בקצה ארץ׃ 24
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
כעס לאביו בן כסיל וממר ליולדתו׃ 25
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
גם ענוש לצדיק לא טוב להכות נדיבים על ישר׃ 26
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
חושך אמריו יודע דעת וקר רוח איש תבונה׃ 27
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
גם אויל מחריש חכם יחשב אטם שפתיו נבון׃ 28
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

< מִשְׁלֵי 17 >