< מִשְׁלֵי 17 >
טוב פת חרבה ושלוה בה מבית מלא זבחי ריב׃ | 1 |
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
עבד משכיל ימשל בבן מביש ובתוך אחים יחלק נחלה׃ | 2 |
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
מצרף לכסף וכור לזהב ובחן לבות יהוה׃ | 3 |
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
מרע מקשיב על שפת און שקר מזין על לשון הות׃ | 4 |
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
לעג לרש חרף עשהו שמח לאיד לא ינקה׃ | 5 |
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
עטרת זקנים בני בנים ותפארת בנים אבותם׃ | 6 |
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
לא נאוה לנבל שפת יתר אף כי לנדיב שפת שקר׃ | 7 |
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
אבן חן השחד בעיני בעליו אל כל אשר יפנה ישכיל׃ | 8 |
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
מכסה פשע מבקש אהבה ושנה בדבר מפריד אלוף׃ | 9 |
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
תחת גערה במבין מהכות כסיל מאה׃ | 10 |
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
אך מרי יבקש רע ומלאך אכזרי ישלח בו׃ | 11 |
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
פגוש דב שכול באיש ואל כסיל באולתו׃ | 12 |
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
משיב רעה תחת טובה לא תמיש רעה מביתו׃ | 13 |
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
פוטר מים ראשית מדון ולפני התגלע הריב נטוש׃ | 14 |
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
מצדיק רשע ומרשיע צדיק תועבת יהוה גם שניהם׃ | 15 |
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
למה זה מחיר ביד כסיל לקנות חכמה ולב אין׃ | 16 |
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
בכל עת אהב הרע ואח לצרה יולד׃ | 17 |
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
אדם חסר לב תוקע כף ערב ערבה לפני רעהו׃ | 18 |
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
אהב פשע אהב מצה מגביה פתחו מבקש שבר׃ | 19 |
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
עקש לב לא ימצא טוב ונהפך בלשונו יפול ברעה׃ | 20 |
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
ילד כסיל לתוגה לו ולא ישמח אבי נבל׃ | 21 |
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
לב שמח ייטב גהה ורוח נכאה תיבש גרם׃ | 22 |
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
שחד מחיק רשע יקח להטות ארחות משפט׃ | 23 |
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
את פני מבין חכמה ועיני כסיל בקצה ארץ׃ | 24 |
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
כעס לאביו בן כסיל וממר ליולדתו׃ | 25 |
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
גם ענוש לצדיק לא טוב להכות נדיבים על ישר׃ | 26 |
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
חושך אמריו יודע דעת וקר רוח איש תבונה׃ | 27 |
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
גם אויל מחריש חכם יחשב אטם שפתיו נבון׃ | 28 |
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.