< מִשְׁלֵי 11 >
מאזני מרמה תועבת יהוה ואבן שלמה רצונו׃ | 1 |
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
בא זדון ויבא קלון ואת צנועים חכמה׃ | 2 |
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
תמת ישרים תנחם וסלף בוגדים ושדם׃ | 3 |
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
לא יועיל הון ביום עברה וצדקה תציל ממות׃ | 4 |
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
צדקת תמים תישר דרכו וברשעתו יפל רשע׃ | 5 |
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
צדקת ישרים תצילם ובהות בגדים ילכדו׃ | 6 |
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
במות אדם רשע תאבד תקוה ותוחלת אונים אבדה׃ | 7 |
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
צדיק מצרה נחלץ ויבא רשע תחתיו׃ | 8 |
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
בפה חנף ישחת רעהו ובדעת צדיקים יחלצו׃ | 9 |
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
בטוב צדיקים תעלץ קריה ובאבד רשעים רנה׃ | 10 |
Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
בברכת ישרים תרום קרת ובפי רשעים תהרס׃ | 11 |
Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
בז לרעהו חסר לב ואיש תבונות יחריש׃ | 12 |
Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
הולך רכיל מגלה סוד ונאמן רוח מכסה דבר׃ | 13 |
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
באין תחבלות יפל עם ותשועה ברב יועץ׃ | 14 |
Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
רע ירוע כי ערב זר ושנא תקעים בוטח׃ | 15 |
Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
אשת חן תתמך כבוד ועריצים יתמכו עשר׃ | 16 |
Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
גמל נפשו איש חסד ועכר שארו אכזרי׃ | 17 |
Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
רשע עשה פעלת שקר וזרע צדקה שכר אמת׃ | 18 |
Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
כן צדקה לחיים ומרדף רעה למותו׃ | 19 |
Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
תועבת יהוה עקשי לב ורצונו תמימי דרך׃ | 20 |
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
יד ליד לא ינקה רע וזרע צדיקים נמלט׃ | 21 |
Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
נזם זהב באף חזיר אשה יפה וסרת טעם׃ | 22 |
Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
תאות צדיקים אך טוב תקות רשעים עברה׃ | 23 |
Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
יש מפזר ונוסף עוד וחושך מישר אך למחסור׃ | 24 |
Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
נפש ברכה תדשן ומרוה גם הוא יורא׃ | 25 |
Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
מנע בר יקבהו לאום וברכה לראש משביר׃ | 26 |
Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
שחר טוב יבקש רצון ודרש רעה תבואנו׃ | 27 |
Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
בוטח בעשרו הוא יפל וכעלה צדיקים יפרחו׃ | 28 |
Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
עוכר ביתו ינחל רוח ועבד אויל לחכם לב׃ | 29 |
Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
פרי צדיק עץ חיים ולקח נפשות חכם׃ | 30 |
Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
הן צדיק בארץ ישלם אף כי רשע וחוטא׃ | 31 |
Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!