< איוב 5 >

קרא נא היש עונך ואל מי מקדשים תפנה׃ 1
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
כי לאויל יהרג כעש ופתה תמית קנאה׃ 2
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
אני ראיתי אויל משריש ואקוב נוהו פתאם׃ 3
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
ירחקו בניו מישע וידכאו בשער ואין מציל׃ 4
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
אשר קצירו רעב יאכל ואל מצנים יקחהו ושאף צמים חילם׃ 5
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
כי לא יצא מעפר און ומאדמה לא יצמח עמל׃ 6
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
כי אדם לעמל יולד ובני רשף יגביהו עוף׃ 7
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
אולם אני אדרש אל אל ואל אלהים אשים דברתי׃ 8
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
עשה גדלות ואין חקר נפלאות עד אין מספר׃ 9
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
הנתן מטר על פני ארץ ושלח מים על פני חוצות׃ 10
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
לשום שפלים למרום וקדרים שגבו ישע׃ 11
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
מפר מחשבות ערומים ולא תעשינה ידיהם תושיה׃ 12
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
לכד חכמים בערמם ועצת נפתלים נמהרה׃ 13
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
יומם יפגשו חשך וכלילה ימששו בצהרים׃ 14
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
וישע מחרב מפיהם ומיד חזק אביון׃ 15
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
ותהי לדל תקוה ועלתה קפצה פיה׃ 16
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
הנה אשרי אנוש יוכחנו אלוה ומוסר שדי אל תמאס׃ 17
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
כי הוא יכאיב ויחבש ימחץ וידו תרפינה׃ 18
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
בשש צרות יצילך ובשבע לא יגע בך רע׃ 19
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
ברעב פדך ממות ובמלחמה מידי חרב׃ 20
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
בשוט לשון תחבא ולא תירא משד כי יבוא׃ 21
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
לשד ולכפן תשחק ומחית הארץ אל תירא׃ 22
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
כי עם אבני השדה בריתך וחית השדה השלמה לך׃ 23
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
וידעת כי שלום אהלך ופקדת נוך ולא תחטא׃ 24
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
וידעת כי רב זרעך וצאצאיך כעשב הארץ׃ 25
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
תבוא בכלח אלי קבר כעלות גדיש בעתו׃ 26
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
הנה זאת חקרנוה כן היא שמענה ואתה דע לך׃ 27
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< איוב 5 >