< איוב 20 >
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
לכן שעפי ישיבוני ובעבור חושי בי׃ | 2 |
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
מוסר כלמתי אשמע ורוח מבינתי יענני׃ | 3 |
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
הזאת ידעת מני עד מני שים אדם עלי ארץ׃ | 4 |
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
כי רננת רשעים מקרוב ושמחת חנף עדי רגע׃ | 5 |
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
אם יעלה לשמים שיאו וראשו לעב יגיע׃ | 6 |
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
כגללו לנצח יאבד ראיו יאמרו איו׃ | 7 |
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
כחלום יעוף ולא ימצאוהו וידד כחזיון לילה׃ | 8 |
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
עין שזפתו ולא תוסיף ולא עוד תשורנו מקומו׃ | 9 |
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
בניו ירצו דלים וידיו תשבנה אונו׃ | 10 |
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
עצמותיו מלאו עלומו ועמו על עפר תשכב׃ | 11 |
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
אם תמתיק בפיו רעה יכחידנה תחת לשונו׃ | 12 |
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
יחמל עליה ולא יעזבנה וימנענה בתוך חכו׃ | 13 |
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
לחמו במעיו נהפך מרורת פתנים בקרבו׃ | 14 |
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
חיל בלע ויקאנו מבטנו יורשנו אל׃ | 15 |
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
ראש פתנים יינק תהרגהו לשון אפעה׃ | 16 |
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
אל ירא בפלגות נהרי נחלי דבש וחמאה׃ | 17 |
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
משיב יגע ולא יבלע כחיל תמורתו ולא יעלס׃ | 18 |
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
כי רצץ עזב דלים בית גזל ולא יבנהו׃ | 19 |
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
כי לא ידע שלו בבטנו בחמודו לא ימלט׃ | 20 |
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
אין שריד לאכלו על כן לא יחיל טובו׃ | 21 |
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
במלאות שפקו יצר לו כל יד עמל תבואנו׃ | 22 |
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
יהי למלא בטנו ישלח בו חרון אפו וימטר עלימו בלחומו׃ | 23 |
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
יברח מנשק ברזל תחלפהו קשת נחושה׃ | 24 |
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
שלף ויצא מגוה וברק ממררתו יהלך עליו אמים׃ | 25 |
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
כל חשך טמון לצפוניו תאכלהו אש לא נפח ירע שריד באהלו׃ | 26 |
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
יגלו שמים עונו וארץ מתקוממה לו׃ | 27 |
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
יגל יבול ביתו נגרות ביום אפו׃ | 28 |
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
זה חלק אדם רשע מאלהים ונחלת אמרו מאל׃ | 29 |
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”