< תהילים 6 >
לַמְנַצֵּחַ בִּנְגִינוֹת עַֽל־הַשְּׁמִינִית מִזְמוֹר לְדָוִֽד׃ יְֽהֹוָה אַל־בְּאַפְּךָ תוֹכִיחֵנִי וְֽאַל־בַּחֲמָתְךָ תְיַסְּרֵֽנִי׃ | 1 |
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
חׇנֵּנִי יְהֹוָה כִּי אֻמְלַל ־ אָנִי רְפָאֵנִי יְהֹוָה כִּי נִבְהֲלוּ עֲצָמָֽי׃ | 2 |
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
וְנַפְשִׁי נִבְהֲלָה מְאֹד (ואת) [וְאַתָּה] יְהֹוָה עַד־מָתָֽי׃ | 3 |
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
שׁוּבָה יְהֹוָה חַלְּצָה נַפְשִׁי הוֹשִׁיעֵנִי לְמַעַן חַסְדֶּֽךָ׃ | 4 |
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
כִּי אֵין בַּמָּוֶת זִכְרֶךָ בִּשְׁאוֹל מִי יֽוֹדֶה־לָּֽךְ׃ (Sheol ) | 5 |
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
יָגַעְתִּי ׀ בְּֽאַנְחָתִי אַשְׂחֶה בְכׇל־לַיְלָה מִטָּתִי בְּדִמְעָתִי עַרְשִׂי אַמְסֶֽה׃ | 6 |
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
עָשְׁשָׁה מִכַּעַס עֵינִי עָתְקָה בְּכׇל־צוֹרְרָֽי׃ | 7 |
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
סוּרוּ מִמֶּנִּי כׇּל־פֹּעֲלֵי אָוֶן כִּֽי־שָׁמַע יְהֹוָה קוֹל בִּכְיִֽי׃ | 8 |
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
שָׁמַע יְהֹוָה תְּחִנָּתִי יְהֹוָה תְּֽפִלָּתִי יִקָּֽח׃ | 9 |
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
יֵבֹשׁוּ ׀ וְיִבָּהֲלוּ מְאֹד כׇּל־אֹיְבָי יָשֻׁבוּ יֵבֹשׁוּ רָֽגַע׃ | 10 |
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.