< תהילים 90 >
תפלה למשה איש-האלהים אדני--מעון אתה היית לנו בדר ודר | 1 |
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
בטרם הרים ילדו-- ותחולל ארץ ותבל ומעולם עד-עולם אתה אל | 2 |
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
תשב אנוש עד-דכא ותאמר שובו בני-אדם | 3 |
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
כי אלף שנים בעיניך-- כיום אתמול כי יעבר ואשמורה בלילה | 4 |
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
זרמתם שנה יהיו בבקר כחציר יחלף | 5 |
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
בבקר יציץ וחלף לערב ימולל ויבש | 6 |
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
כי-כלינו באפך ובחמתך נבהלנו | 7 |
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
שת (שתה) עונתינו לנגדך עלמנו למאור פניך | 8 |
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
כי כל-ימינו פנו בעברתך כלינו שנינו כמו-הגה | 9 |
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
ימי-שנותינו בהם שבעים שנה ואם בגבורת שמונים שנה-- ורהבם עמל ואון כי-גז חיש ונעפה | 10 |
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
מי-יודע עז אפך וכיראתך עברתך | 11 |
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
למנות ימינו כן הודע ונבא לבב חכמה | 12 |
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
שובה יהוה עד-מתי והנחם על-עבדיך | 13 |
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
שבענו בבקר חסדך ונרננה ונשמחה בכל-ימינו | 14 |
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
שמחנו כימות עניתנו שנות ראינו רעה | 15 |
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
יראה אל-עבדיך פעלך והדרך על-בניהם | 16 |
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
ויהי נעם אדני אלהינו-- עלינו ומעשה ידינו כוננה עלינו ומעשה ידינו כוננהו | 17 |
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.