< תהילים 9 >
למנצח על-מות לבן מזמור לדוד ב אודה יהוה בכל-לבי אספרה כל-נפלאותיך | 1 |
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
אשמחה ואעלצה בך אזמרה שמך עליון | 2 |
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
בשוב-אויבי אחור יכשלו ויאבדו מפניך | 3 |
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
כי-עשית משפטי ודיני ישבת לכסא שופט צדק | 4 |
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
גערת גוים אבדת רשע שמם מחית לעולם ועד | 5 |
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
האויב תמו חרבות--לנצח וערים נתשת--אבד זכרם המה | 6 |
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
ויהוה לעולם ישב כונן למשפט כסאו | 7 |
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
והוא ישפט-תבל בצדק ידין לאמים במישרים | 8 |
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
ויהי יהוה משגב לדך משגב לעתות בצרה | 9 |
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
ויבטחו בך יודעי שמך כי לא-עזבת דרשיך יהוה | 10 |
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
זמרו--ליהוה ישב ציון הגידו בעמים עלילותיו | 11 |
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
כי-דרש דמים אותם זכר לא-שכח צעקת עניים (ענוים) | 12 |
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
חננני יהוה--ראה עניי משנאי מרוממי משערי מות | 13 |
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
למען אספרה כל-תהלתיך בשערי בת-ציון--אגילה בישועתך | 14 |
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
טבעו גוים בשחת עשו ברשת-זו טמנו נלכדה רגלם | 15 |
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
נודע יהוה--משפט עשה בפעל כפיו נוקש רשע הגיון סלה | 16 |
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
ישובו רשעים לשאולה כל-גוים שכחי אלהים (Sheol ) | 17 |
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol )
כי לא לנצח ישכח אביון תקות ענוים (עניים) תאבד לעד | 18 |
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
קומה יהוה אל-יעז אנוש ישפטו גוים על-פניך | 19 |
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
שיתה יהוה מורה--להם ידעו גוים--אנוש המה סלה | 20 |
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)