< תהילים 89 >
משכיל לאיתן האזרחי ב חסדי יהוה עולם אשירה לדר ודר אודיע אמונתך בפי | 1 |
Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara. Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya; ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.
כי-אמרתי--עולם חסד יבנה שמים תכן אמונתך בהם | 2 |
Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya, kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.
כרתי ברית לבחירי נשבעתי לדוד עבדי | 3 |
Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga, ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,
עד-עולם אכין זרעך ובניתי לדר-ודור כסאך סלה | 4 |
‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya. Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’” (Sela)
ויודו שמים פלאך יהוה אף-אמונתך בקהל קדשים | 5 |
Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova, kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.
כי מי בשחק יערך ליהוה ידמה ליהוה בבני אלים | 6 |
Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova? Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?
אל נערץ בסוד-קדשים רבה ונורא על-כל-סביביו | 7 |
Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri; Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.
יהוה אלהי צבאות--מי-כמוך חסין יה ואמונתך סביבותיך | 8 |
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu? Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.
אתה מושל בגאות הים בשוא גליו אתה תשבחם | 9 |
Mumalamula nyanja ya mafunde awukali; pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.
אתה דכאת כחלל רהב בזרוע עזך פזרת אויביך | 10 |
Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa; ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.
לך שמים אף-לך ארץ תבל ומלאה אתה יסדתם | 11 |
Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu; munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.
צפון וימין אתה בראתם תבור וחרמון בשמך ירננו | 12 |
Munalenga Kumpoto ndi Kummwera; Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.
לך זרוע עם-גבורה תעז ידך תרום ימינך | 13 |
Mkono wanu ndi wamphamvu; dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.
צדק ומשפט מכון כסאך חסד ואמת יקדמו פניך | 14 |
Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu; chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.
אשרי העם ידעי תרועה יהוה באור-פניך יהלכון | 15 |
Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu, amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.
בשמך יגילון כל-היום ובצדקתך ירומו | 16 |
Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu; amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.
כי-תפארת עזמו אתה וברצונך תרים (תרום) קרנינו | 17 |
Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.
כי ליהוה מגננו ולקדוש ישראל מלכנו | 18 |
Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova, Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.
אז דברת בחזון לחסידיך-- ותאמר שויתי עזר על-גבור הרימותי בחור מעם | 19 |
Kale munayankhula mʼmasomphenya, kwa anthu anu okhulupirika munati, “Ndapatsa mphamvu wankhondo; ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.
מצאתי דוד עבדי בשמן קדשי משחתיו | 20 |
Ndamupeza mtumiki wanga Davide; ndamudzoza ndi mafuta opatulika.
אשר ידי תכון עמו אף-זרועי תאמצנו | 21 |
Dzanja langa lidzamuchirikiza; zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.
לא-ישיא אויב בו ובן-עולה לא יעננו | 22 |
Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho; anthu oyipa sadzamusautsa.
וכתותי מפניו צריו ומשנאיו אגוף | 23 |
Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake ndi kukantha otsutsana naye.
ואמונתי וחסדי עמו ובשמי תרום קרנו | 24 |
Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye, ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.
ושמתי בים ידו ובנהרות ימינו | 25 |
Ndidzayika dzanja lake pa nyanja, dzanja lake lamanja pa mitsinje.
הוא יקראני אבי אתה אלי וצור ישועתי | 26 |
Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga, Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’
אף-אני בכור אתנהו עליון למלכי-ארץ | 27 |
Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa; wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.
לעולם אשמור- (אשמר-) לו חסדי ובריתי נאמנת לו | 28 |
Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya, ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.
ושמתי לעד זרעו וכסאו כימי שמים | 29 |
Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya, mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.
אם-יעזבו בניו תורתי ובמשפטי לא ילכון | 30 |
“Ngati ana ake adzataya lamulo langa ndi kusatsatira malangizo anga,
אם-חקתי יחללו ומצותי לא ישמרו | 31 |
ngati adzaswa malamulo anga ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,
ופקדתי בשבט פשעם ובנגעים עונם | 32 |
Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo, mphulupulu zawo powakwapula.
וחסדי לא-אפיר מעמו ולא-אשקר באמונתי | 33 |
Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye, kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.
לא-אחלל בריתי ומוצא שפתי לא אשנה | 34 |
Sindidzaswa pangano langa kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.
אחת נשבעתי בקדשי אם-לדוד אכזב | 35 |
Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga ndipo sindidzanama kwa Davide,
זרעו לעולם יהיה וכסאו כשמש נגדי | 36 |
kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;
כירח יכון עולם ועד בשחק נאמן סלה | 37 |
udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi, mboni yokhulupirika mʼmitambo. (Sela)
ואתה זנחת ותמאס התעברת עם-משיחך | 38 |
“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya, mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.
נארתה ברית עבדך חללת לארץ נזרו | 39 |
Mwakana pangano ndi mtumiki wanu ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.
פרצת כל-גדרתיו שמת מבצריו מחתה | 40 |
Inu mwagumula makoma ake onse ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.
שסהו כל-עברי דרך היה חרפה לשכניו | 41 |
Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake; iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.
הרימות ימין צריו השמחת כל-אויביו | 42 |
Mwakweza dzanja lamanja la adani ake; mwachititsa kuti adani ake akondwere.
אף-תשיב צור חרבו ולא הקימתו במלחמה | 43 |
Mwabunthitsa lupanga lake, simunamuthandize pa nkhondo.
השבת מטהרו וכסאו לארץ מגרתה | 44 |
Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.
הקצרת ימי עלומיו העטית עליו בושה סלה | 45 |
Mwachepetsa masiku a unyamata wake; mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi. (Sela)
עד-מה יהוה תסתר לנצח תבער כמו-אש חמתך | 46 |
“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale? Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?
זכר-אני מה-חלד על-מה-שוא בראת כל-בני-אדם | 47 |
Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa pakuti munalenga kwachabe anthu onse!
מי גבר יחיה ולא יראה-מות ימלט נפשו מיד-שאול סלה (Sheol ) | 48 |
Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? (Sela) (Sheol )
איה חסדיך הראשנים אדני נשבעת לדוד באמונתך | 49 |
Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija, chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?
זכר אדני חרפת עבדיך שאתי בחיקי כל-רבים עמים | 50 |
Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera, momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,
אשר חרפו אויביך יהוה אשר חרפו עקבות משיחך | 51 |
mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova, ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.
ברוך יהוה לעולם אמן ואמן | 52 |
“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”