< תהילים 78 >

משכיל לאסף האזינה עמי תורתי הטו אזנכם לאמרי-פי 1
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
אפתחה במשל פי אביעה חידות מני-קדם 2
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
אשר שמענו ונדעם ואבותינו ספרו-לנו 3
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
לא נכחד מבניהם-- לדור אחרון מספרים תהלות יהוה ועזוזו ונפלאתיו אשר עשה 4
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
ויקם עדות ביעקב ותורה שם בישראל אשר צוה את-אבותינו-- להודיעם לבניהם 5
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
למען ידעו דור אחרון--בנים יולדו יקמו ויספרו לבניהם 6
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
וישימו באלהים כסלם ולא ישכחו מעללי-אל ומצותיו ינצרו 7
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
ולא יהיו כאבותם-- דור סורר ומרה דור לא-הכין לבו ולא-נאמנה את-אל רוחו 8
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
בני-אפרים נושקי רומי-קשת הפכו ביום קרב 9
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
לא שמרו ברית אלהים ובתורתו מאנו ללכת 10
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
וישכחו עלילותיו ונפלאותיו אשר הראם 11
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
נגד אבותם עשה פלא בארץ מצרים שדה-צען 12
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
בקע ים ויעבירם ויצב-מים כמו-נד 13
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
וינחם בענן יומם וכל-הלילה באור אש 14
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
יבקע צרים במדבר וישק כתהמות רבה 15
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
ויוצא נוזלים מסלע ויורד כנהרות מים 16
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
ויוסיפו עוד לחטא-לו-- למרות עליון בציה 17
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
וינסו-אל בלבבם-- לשאל-אכל לנפשם 18
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
וידברו באלהים אמרו היוכל אל--לערך שלחן במדבר 19
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
הן הכה-צור ויזובו מים-- ונחלים ישטפו הגם-לחם יוכל תת אם-יכין שאר לעמו 20
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
לכן שמע יהוה-- ויתעבר ואש נשקה ביעקב וגם-אף עלה בישראל 21
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
כי לא האמינו באלהים ולא בטחו בישועתו 22
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
ויצו שחקים ממעל ודלתי שמים פתח 23
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
וימטר עליהם מן לאכל ודגן-שמים נתן למו 24
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
לחם אבירים אכל איש צידה שלח להם לשבע 25
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
יסע קדים בשמים וינהג בעזו תימן 26
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
וימטר עליהם כעפר שאר וכחול ימים עוף כנף 27
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
ויפל בקרב מחנהו סביב למשכנתיו 28
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
ויאכלו וישבעו מאד ותאותם יבא להם 29
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
לא-זרו מתאותם עוד אכלם בפיהם 30
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
ואף אלהים עלה בהם ויהרג במשמניהם ובחורי ישראל הכריע 31
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
בכל-זאת חטאו-עוד ולא-האמינו בנפלאותיו 32
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
ויכל-בהבל ימיהם ושנותם בבהלה 33
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
אם-הרגם ודרשוהו ושבו ושחרו-אל 34
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
ויזכרו כי-אלהים צורם ואל עליון גאלם 35
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
ויפתוהו בפיהם ובלשונם יכזבו-לו 36
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
ולבם לא-נכון עמו ולא נאמנו בבריתו 37
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
והוא רחום יכפר עון-- ולא-ישחית והרבה להשיב אפו ולא-יעיר כל-חמתו 38
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
ויזכר כי-בשר המה רוח הולך ולא ישוב 39
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
כמה ימרוהו במדבר יעציבוהו בישימון 40
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
וישובו וינסו אל וקדוש ישראל התוו 41
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
לא-זכרו את-ידו יום אשר-פדם מני-צר 42
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
אשר-שם במצרים אתותיו ומופתיו בשדה-צען 43
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
ויהפך לדם יאריהם ונזליהם בל-ישתיון 44
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
ישלח בהם ערב ויאכלם וצפרדע ותשחיתם 45
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
ויתן לחסיל יבולם ויגיעם לארבה 46
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
יהרג בברד גפנם ושקמותם בחנמל 47
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
ויסגר לברד בעירם ומקניהם לרשפים 48
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
ישלח-בם חרון אפו--עברה וזעם וצרה משלחת מלאכי רעים 49
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
יפלס נתיב לאפו לא-חשך ממות נפשם וחיתם לדבר הסגיר 50
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
ויך כל-בכור במצרים ראשית אונים באהלי-חם 51
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
ויסע כצאן עמו וינהגם כעדר במדבר 52
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
וינחם לבטח ולא פחדו ואת-אויביהם כסה הים 53
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
ויביאם אל-גבול קדשו הר-זה קנתה ימינו 54
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
ויגרש מפניהם גוים-- ויפילם בחבל נחלה וישכן באהליהם שבטי ישראל 55
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
וינסו וימרו את-אלהים עליון ועדותיו לא שמרו 56
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
ויסגו ויבגדו כאבותם נהפכו כקשת רמיה 57
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
ויכעיסוהו בבמותם ובפסיליהם יקניאוהו 58
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
שמע אלהים ויתעבר וימאס מאד בישראל 59
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
ויטש משכן שלו אהל שכן באדם 60
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
ויתן לשבי עזו ותפארתו ביד-צר 61
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
ויסגר לחרב עמו ובנחלתו התעבר 62
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
בחוריו אכלה-אש ובתולתיו לא הוללו 63
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
כהניו בחרב נפלו ואלמנתיו לא תבכינה 64
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
ויקץ כישן אדני כגבור מתרונן מיין 65
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
ויך-צריו אחור חרפת עולם נתן למו 66
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
וימאס באהל יוסף ובשבט אפרים לא בחר 67
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
ויבחר את-שבט יהודה את-הר ציון אשר אהב 68
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
ויבן כמו-רמים מקדשו כארץ יסדה לעולם 69
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
ויבחר בדוד עבדו ויקחהו ממכלאת צאן 70
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
מאחר עלות הביאו לרעות ביעקב עמו ובישראל נחלתו 71
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
וירעם כתם לבבו ובתבונות כפיו ינחם 72
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< תהילים 78 >