< תהילים 76 >

למנצח בנגינת מזמור לאסף שיר ב נודע ביהודה אלהים בישראל גדול שמו 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
ויהי בשלם סוכו ומעונתו בציון 2
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
שמה שבר רשפי-קשת מגן וחרב ומלחמה סלה 3
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
נאור אתה אדיר-- מהררי-טרף 4
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
אשתוללו אבירי לב-- נמו שנתם ולא-מצאו כל-אנשי-חיל ידיהם 5
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
מגערתך אלהי יעקב נרדם ורכב וסוס 6
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
אתה נורא אתה--ומי-יעמד לפניך מאז אפך 7
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
משמים השמעת דין ארץ יראה ושקטה 8
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
בקום-למשפט אלהים-- להושיע כל-ענוי-ארץ סלה 9
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
כי-חמת אדם תודך שארית חמת תחגר 10
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
נדרו ושלמו ליהוה אלהיכם כל-סביביו--יבילו שי למורא 11
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
יבצר רוח נגידים נורא למלכי-ארץ 12
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< תהילים 76 >