< תהילים 64 >

למנצח מזמור לדוד ב שמע-אלהים קולי בשיחי מפחד אויב תצר חיי 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
תסתירני מסוד מרעים מרגשת פעלי און 2
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
אשר שננו כחרב לשונם דרכו חצם דבר מר 3
Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
לירת במסתרים תם פתאם ירהו ולא ייראו 4
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
יחזקו-למו דבר רע-- יספרו לטמון מוקשים אמרו מי יראה-למו 5
Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
יחפשו עולת-- תמנו חפש מחפש וקרב איש ולב עמק 6
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
וירם אלהים חץ פתאום--היו מכותם 7
Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
ויכשילוהו עלימו לשונם יתנדדו כל-ראה בם 8
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
וייראו כל-אדם ויגידו פעל אלהים ומעשהו השכילו 9
Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
ישמח צדיק ביהוה וחסה בו ויתהללו כל-ישרי-לב 10
Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!

< תהילים 64 >