< תהילים 61 >
למנצח על-נגינת לדוד ב שמעה אלהים רנתי הקשיבה תפלתי | 1 |
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
מקצה הארץ אליך אקרא-- בעטף לבי בצור-ירום ממני תנחני | 2 |
Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
כי-היית מחסה לי מגדל-עז מפני אויב | 3 |
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
אגורה באהלך עולמים אחסה בסתר כנפיך סלה | 4 |
Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
כי-אתה אלהים שמעת לנדרי נתת ירשת יראי שמך | 5 |
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
ימים על-ימי-מלך תוסיף שנותיו כמו-דר ודר | 6 |
Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
ישב עולם לפני אלהים חסד ואמת מן ינצרהו | 7 |
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
כן אזמרה שמך לעד-- לשלמי נדרי יום יום | 8 |
Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.