< תהילים 38 >

מזמור לדוד להזכיר ב יהוה--אל-בקצפך תוכיחני ובחמתך תיסרני 1
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
כי-חציך נחתו בי ותנחת עלי ידך 2
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
אין-מתם בבשרי מפני זעמך אין-שלום בעצמי מפני חטאתי 3
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
כי עונתי עברו ראשי כמשא כבד יכבדו ממני 4
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
הבאישו נמקו חבורתי מפני אולתי 5
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
נעויתי שחתי עד-מאד כל-היום קדר הלכתי 6
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
כי-כסלי מלאו נקלה ואין מתם בבשרי 7
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
נפוגותי ונדכיתי עד-מאד שאגתי מנהמת לבי 8
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
אדני נגדך כל-תאותי ואנחתי ממך לא-נסתרה 9
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
לבי סחרחר עזבני כחי ואור-עיני גם-הם אין אתי 10
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
אהבי ורעי--מנגד נגעי יעמדו וקרובי מרחק עמדו 11
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
וינקשו מבקשי נפשי ודרשי רעתי דברו הוות ומרמות כל-היום יהגו 12
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
ואני כחרש לא אשמע וכאלם לא יפתח-פיו 13
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
ואהי--כאיש אשר לא-שמע ואין בפיו תוכחות 14
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
כי-לך יהוה הוחלתי אתה תענה אדני אלהי 15
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
כי-אמרתי פן-ישמחו-לי במוט רגלי עלי הגדילו 16
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
כי-אני לצלע נכון ומכאובי נגדי תמיד 17
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
כי-עוני אגיד אדאג מחטאתי 18
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
ואיבי חיים עצמו ורבו שנאי שקר 19
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
ומשלמי רעה תחת טובה-- ישטנוני תחת רדופי- (רדפי-) טוב 20
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
אל-תעזבני יהוה אלהי אל-תרחק ממני 21
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
חושה לעזרתי אדני תשועתי 22
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< תהילים 38 >