< תהילים 30 >

מזמור שיר-חנכת הבית לדוד ב ארוממך יהוה כי דליתני ולא-שמחת איבי לי 1
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
יהוה אלהי-- שועתי אליך ותרפאני 2
Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
יהוה--העלית מן-שאול נפשי חייתני מיורדי- (מירדי-) בור (Sheol h7585) 3
Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
זמרו ליהוה חסידיו והודו לזכר קדשו 4
Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
כי רגע באפו-- חיים ברצונו בערב ילין בכי ולבקר רנה 5
Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
ואני אמרתי בשלוי-- בל-אמוט לעולם 6
Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
יהוה-- ברצונך העמדתה להררי-עז הסתרת פניך הייתי נבהל 7
Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
אליך יהוה אקרא ואל-אדני אתחנן 8
Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
מה-בצע בדמי ברדתי אל-שחת היודך עפר היגיד אמתך 9
“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
שמע-יהוה וחנני יהוה היה-עזר לי 10
Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
הפכת מספדי למחול לי פתחת שקי ותאזרני שמחה 11
Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
למען יזמרך כבוד-- ולא ידם יהוה אלהי לעולם אודך 12
kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

< תהילים 30 >