< תהילים 26 >

לדוד שפטני יהוה-- כי-אני בתמי הלכתי וביהוה בטחתי לא אמעד 1
Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
בחנני יהוה ונסני צרופה (צרפה) כליותי ולבי 2
Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
כי-חסדך לנגד עיני והתהלכתי באמתך 3
pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
לא-ישבתי עם-מתי-שוא ועם נעלמים לא אבוא 4
Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
שנאתי קהל מרעים ועם-רשעים לא אשב 5
Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
ארחץ בנקיון כפי ואסבבה את-מזבחך יהוה 6
Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
לשמע בקול תודה ולספר כל-נפלאותיך 7
kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
יהוה--אהבתי מעון ביתך ומקום משכן כבודך 8
Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
אל-תאסף עם-חטאים נפשי ועם-אנשי דמים חיי 9
Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
אשר-בידיהם זמה וימינם מלאה שחד 10
amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
ואני בתמי אלך פדני וחנני 11
Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
רגלי עמדה במישור במקהלים אברך יהוה 12
Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.

< תהילים 26 >