< תהילים 147 >
הללו-יה כי-טוב זמרה אלהינו-- כי-נעים נאוה תהלה | 1 |
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
בונה ירושלם יהוה נדחי ישראל יכנס | 2 |
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
הרפא לשבורי לב ומחבש לעצבותם | 3 |
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
מונה מספר לכוכבים לכלם שמות יקרא | 4 |
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
גדול אדונינו ורב-כח לתבונתו אין מספר | 5 |
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
מעודד ענוים יהוה משפיל רשעים עדי-ארץ | 6 |
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
ענו ליהוה בתודה זמרו לאלהינו בכנור | 7 |
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
המכסה שמים בעבים-- המכין לארץ מטר המצמיח הרים חציר | 8 |
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
נותן לבהמה לחמה לבני ערב אשר יקראו | 9 |
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
לא בגבורת הסוס יחפץ לא-בשוקי האיש ירצה | 10 |
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
רוצה יהוה את-יראיו-- את-המיחלים לחסדו | 11 |
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
שבחי ירושלם את-יהוה הללי אלהיך ציון | 12 |
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
כי-חזק בריחי שעריך ברך בניך בקרבך | 13 |
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
השם-גבולך שלום חלב חטים ישביעך | 14 |
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
השלח אמרתו ארץ עד-מהרה ירוץ דברו | 15 |
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
הנתן שלג כצמר כפור כאפר יפזר | 16 |
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
משליך קרחו כפתים לפני קרתו מי יעמד | 17 |
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
ישלח דברו וימסם ישב רוחו יזלו-מים | 18 |
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
מגיד דברו ליעקב חקיו ומשפטיו לישראל | 19 |
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
לא עשה כן לכל-גוי-- ומשפטים בל-ידעום הללו-יה | 20 |
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.