< תהילים 144 >
לדוד ברוך יהוה צורי-- המלמד ידי לקרב אצבעותי למלחמה | 1 |
Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
חסדי ומצודתי משגבי ומפלטי-לי מגני ובו חסיתי הרודד עמי תחתי | 2 |
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
יהוה--מה-אדם ותדעהו בן-אנוש ותחשבהו | 3 |
Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
אדם להבל דמה ימיו כצל עובר | 4 |
Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
יהוה הט-שמיך ותרד גע בהרים ויעשנו | 5 |
Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
ברוק ברק ותפיצם שלח חציך ותהמם | 6 |
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
שלח ידיך ממרום פצני והצילני ממים רבים מיד בני נכר | 7 |
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
אשר פיהם דבר-שוא וימינם ימין שקר | 8 |
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
אלהים--שיר חדש אשירה לך בנבל עשור אזמרה-לך | 9 |
Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
הנותן תשועה למלכים הפוצה את-דוד עבדו--מחרב רעה | 10 |
kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
פצני והצילני מיד בני-נכר אשר פיהם דבר-שוא וימינם ימין שקר | 11 |
Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
אשר בנינו כנטעים-- מגדלים בנעוריהם בנותינו כזוית-- מחטבות תבנית היכל | 12 |
Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
מזוינו מלאים-- מפיקים מזן אל-זן צאוננו מאליפות מרבבות-- בחוצותינו | 13 |
Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
אלופינו מסבלים אין-פרץ ואין יוצאת ואין צוחה ברחבתינו | 14 |
Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
אשרי העם שככה לו אשרי העם שיהוה אלהיו | 15 |
Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.