< תהילים 143 >
מזמור לדוד יהוה שמע תפלתי-- האזינה אל-תחנוני באמנתך ענני בצדקתך | 1 |
Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
ואל-תבוא במשפט את-עבדך כי לא-יצדק לפניך כל-חי | 2 |
Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
כי רדף אויב נפשי-- דכא לארץ חיתי הושבני במחשכים כמתי עולם | 3 |
Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
ותתעטף עלי רוחי בתוכי ישתומם לבי | 4 |
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
זכרתי ימים מקדם-- הגיתי בכל-פעלך במעשה ידיך אשוחח | 5 |
Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
פרשתי ידי אליך נפשי כארץ-עיפה לך סלה | 6 |
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
מהר ענני יהוה-- כלתה רוחי אל-תסתר פניך ממני ונמשלתי עם-ירדי בור | 7 |
Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
השמיעני בבקר חסדך-- כי-בך בטחתי הודיעני דרך-זו אלך-- כי-אליך נשאתי נפשי | 8 |
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
הצילני מאיבי יהוה-- אליך כסתי | 9 |
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
למדני לעשות רצונך-- כי-אתה אלוהי רוחך טובה תנחני בארץ מישור | 10 |
Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
למען-שמך יהוה תחיני בצדקתך תוציא מצרה נפשי | 11 |
Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
ובחסדך תצמית איבי והאבדת כל-צררי נפשי--כי אני עבדך | 12 |
Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.