< תהילים 119 >
אשרי תמימי-דרך-- ההלכים בתורת יהוה | 1 |
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
אשרי נצרי עדתיו בכל-לב ידרשוהו | 2 |
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
אף לא-פעלו עולה בדרכיו הלכו | 3 |
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
אתה צויתה פקדיך-- לשמר מאד | 4 |
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
אחלי יכנו דרכי-- לשמר חקיך | 5 |
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
אז לא-אבוש-- בהביטי אל-כל-מצותיך | 6 |
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
אודך בישר לבב-- בלמדי משפטי צדקך | 7 |
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
את-חקיך אשמר אל-תעזבני עד-מאד | 8 |
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
במה יזכה-נער את-ארחו-- לשמר כדברך | 9 |
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
בכל-לבי דרשתיך אל-תשגני ממצותיך | 10 |
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
בלבי צפנתי אמרתך-- למען לא אחטא-לך | 11 |
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
ברוך אתה יהוה-- למדני חקיך | 12 |
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
בשפתי ספרתי-- כל משפטי-פיך | 13 |
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
בדרך עדותיך ששתי-- כעל כל-הון | 14 |
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
בפקודיך אשיחה ואביטה ארחתיך | 15 |
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
בחקתיך אשתעשע לא אשכח דברך | 16 |
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
גמל על-עבדך אחיה ואשמרה דברך | 17 |
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
גל-עיני ואביטה-- נפלאות מתורתך | 18 |
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
גר אנכי בארץ אל-תסתר ממני מצותיך | 19 |
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
גרסה נפשי לתאבה-- אל-משפטיך בכל-עת | 20 |
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
גערת זדים ארורים-- השגים ממצותיך | 21 |
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
גל מעלי חרפה ובוז כי עדתיך נצרתי | 22 |
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
גם ישבו שרים בי נדברו-- עבדך ישיח בחקיך | 23 |
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
גם-עדתיך שעשעי-- אנשי עצתי | 24 |
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
דבקה לעפר נפשי חיני כדברך | 25 |
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
דרכי ספרתי ותענני למדני חקיך | 26 |
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
דרך-פקודיך הבינני ואשיחה בנפלאותיך | 27 |
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
דלפה נפשי מתוגה קימני כדברך | 28 |
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
דרך-שקר הסר ממני ותורתך חנני | 29 |
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
דרך-אמונה בחרתי משפטיך שויתי | 30 |
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
דבקתי בעדותיך יהוה אל-תבישני | 31 |
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
דרך-מצותיך ארוץ כי תרחיב לבי | 32 |
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
הורני יהוה דרך חקיך ואצרנה עקב | 33 |
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
הבינני ואצרה תורתך ואשמרנה בכל-לב | 34 |
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
הדריכני בנתיב מצותיך כי-בו חפצתי | 35 |
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
הט-לבי אל-עדותיך ואל אל-בצע | 36 |
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
העבר עיני מראות שוא בדרכך חיני | 37 |
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
הקם לעבדך אמרתך-- אשר ליראתך | 38 |
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
העבר חרפתי אשר יגרתי כי משפטיך טובים | 39 |
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
הנה תאבתי לפקדיך בצדקתך חיני | 40 |
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
ויבאני חסדך יהוה תשועתך כאמרתך | 41 |
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
ואענה חרפי דבר כי-בטחתי בדברך | 42 |
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
ואל-תצל מפי דבר-אמת עד-מאד כי למשפטך יחלתי | 43 |
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
ואשמרה תורתך תמיד-- לעולם ועד | 44 |
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
ואתהלכה ברחבה כי פקדיך דרשתי | 45 |
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
ואדברה בעדתיך נגד מלכים ולא אבוש | 46 |
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
ואשתעשע במצותיך אשר אהבתי | 47 |
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
ואשא-כפי--אל-מצותיך אשר אהבתי ואשיחה בחקיך | 48 |
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
זכר-דבר לעבדך-- על אשר יחלתני | 49 |
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
זאת נחמתי בעניי כי אמרתך חיתני | 50 |
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
זדים הליצני עד-מאד מתורתך לא נטיתי | 51 |
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
זכרתי משפטיך מעולם יהוה ואתנחם | 52 |
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
זלעפה אחזתני מרשעים-- עזבי תורתך | 53 |
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
זמרות היו-לי חקיך-- בבית מגורי | 54 |
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
זכרתי בלילה שמך יהוה ואשמרה תורתך | 55 |
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
זאת היתה-לי כי פקדיך נצרתי | 56 |
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
חלקי יהוה אמרתי-- לשמר דבריך | 57 |
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
חליתי פניך בכל-לב חנני כאמרתך | 58 |
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
חשבתי דרכי ואשיבה רגלי אל-עדתיך | 59 |
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
חשתי ולא התמהמהתי-- לשמר מצותיך | 60 |
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
חבלי רשעים עודני תורתך לא שכחתי | 61 |
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
חצות-לילה--אקום להודות לך על משפטי צדקך | 62 |
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
חבר אני לכל-אשר יראוך ולשמרי פקודיך | 63 |
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
חסדך יהוה מלאה הארץ חקיך למדני | 64 |
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
טוב עשית עם-עבדך-- יהוה כדברך | 65 |
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
טוב טעם ודעת למדני כי במצותיך האמנתי | 66 |
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
טרם אענה אני שגג ועתה אמרתך שמרתי | 67 |
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
טוב-אתה ומטיב למדני חקיך | 68 |
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
טפלו עלי שקר זדים אני בכל-לב אצר פקודיך | 69 |
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
טפש כחלב לבם אני תורתך שעשעתי | 70 |
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
טוב-לי כי-עניתי-- למען אלמד חקיך | 71 |
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
טוב-לי תורת-פיך-- מאלפי זהב וכסף | 72 |
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
ידיך עשוני ויכוננוני הבינני ואלמדה מצותיך | 73 |
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
יראיך יראוני וישמחו כי לדברך יחלתי | 74 |
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
ידעתי יהוה כי-צדק משפטיך ואמונה עניתני | 75 |
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
יהי-נא חסדך לנחמני-- כאמרתך לעבדך | 76 |
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
יבאוני רחמיך ואחיה כי-תורתך שעשעי | 77 |
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
יבשו זדים כי-שקר עותוני אני אשיח בפקודיך | 78 |
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
ישובו לי יראיך וידעו (וידעי) עדתיך | 79 |
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
יהי-לבי תמים בחקיך-- למען לא אבוש | 80 |
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
כלתה לתשועתך נפשי לדברך יחלתי | 81 |
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
כלו עיני לאמרתך-- לאמר מתי תנחמני | 82 |
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
כי-הייתי כנאד בקיטור-- חקיך לא שכחתי | 83 |
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
כמה ימי-עבדך מתי תעשה ברדפי משפט | 84 |
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
כרו-לי זדים שיחות-- אשר לא כתורתך | 85 |
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
כל-מצותיך אמונה שקר רדפוני עזרני | 86 |
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
כמעט כלוני בארץ ואני לא-עזבתי פקדיך | 87 |
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
כחסדך חיני ואשמרה עדות פיך | 88 |
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
לעולם יהוה-- דברך נצב בשמים | 89 |
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
לדר ודר אמונתך כוננת ארץ ותעמד | 90 |
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
למשפטיך עמדו היום כי הכל עבדיך | 91 |
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
לולי תורתך שעשעי-- אז אבדתי בעניי | 92 |
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
לעולם לא-אשכח פקודיך כי בם חייתני | 93 |
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
לך-אני הושיעני כי פקודיך דרשתי | 94 |
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
לי קוו רשעים לאבדני עדתיך אתבונן | 95 |
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
לכל-תכלה ראיתי קץ רחבה מצותך מאד | 96 |
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
מה-אהבתי תורתך כל-היום היא שיחתי | 97 |
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
מאיבי תחכמני מצותך כי לעולם היא-לי | 98 |
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
מכל-מלמדי השכלתי כי עדותיך שיחה לי | 99 |
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
מזקנים אתבונן כי פקודיך נצרתי | 100 |
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
מכל-ארח רע כלאתי רגלי-- למען אשמר דברך | 101 |
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
ממשפטיך לא-סרתי כי-אתה הורתני | 102 |
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
מה-נמלצו לחכי אמרתך-- מדבש לפי | 103 |
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
מפקודיך אתבונן על כן שנאתי כל-ארח שקר | 104 |
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
נר-לרגלי דברך ואור לנתיבתי | 105 |
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
נשבעתי ואקימה-- לשמר משפטי צדקך | 106 |
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
נעניתי עד-מאד יהוה חיני כדברך | 107 |
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
נדבות פי רצה-נא יהוה ומשפטיך למדני | 108 |
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
נפשי בכפי תמיד ותורתך לא שכחתי | 109 |
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
נתנו רשעים פח לי ומפקודיך לא תעיתי | 110 |
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
נחלתי עדותיך לעולם כי-ששון לבי המה | 111 |
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
נטיתי לבי לעשות חקיך-- לעולם עקב | 112 |
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
סעפים שנאתי ותורתך אהבתי | 113 |
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
סתרי ומגני אתה לדברך יחלתי | 114 |
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
סורו-ממני מרעים ואצרה מצות אלהי | 115 |
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
סמכני כאמרתך ואחיה ואל-תבישני משברי | 116 |
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
סעדני ואושעה ואשעה בחקיך תמיד | 117 |
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
סלית כל-שוגים מחקיך כי-שקר תרמיתם | 118 |
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
סגים--השבת כל-רשעי-ארץ לכן אהבתי עדתיך | 119 |
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
סמר מפחדך בשרי וממשפטיך יראתי | 120 |
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
עשיתי משפט וצדק בל-תניחני לעשקי | 121 |
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
ערב עבדך לטוב אל-יעשקני זדים | 122 |
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
עיני כלו לישועתך ולאמרת צדקך | 123 |
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
עשה עם-עבדך כחסדך וחקיך למדני | 124 |
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
עבדך-אני הבינני ואדעה עדתיך | 125 |
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
עת לעשות ליהוה-- הפרו תורתך | 126 |
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
על-כן אהבתי מצותיך-- מזהב ומפז | 127 |
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
על-כן כל-פקודי כל ישרתי כל-ארח שקר שנאתי | 128 |
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
פלאות עדותיך על-כן נצרתם נפשי | 129 |
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
פתח דבריך יאיר מבין פתיים | 130 |
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
פי-פערתי ואשאפה כי למצותיך יאבתי | 131 |
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
פנה-אלי וחנני-- כמשפט לאהבי שמך | 132 |
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
פעמי הכן באמרתך ואל-תשלט-בי כל-און | 133 |
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
פדני מעשק אדם ואשמרה פקודיך | 134 |
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
פניך האר בעבדך ולמדני את-חקיך | 135 |
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
פלגי-מים ירדו עיני-- על לא-שמרו תורתך | 136 |
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
צדיק אתה יהוה וישר משפטיך | 137 |
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
צוית צדק עדתיך ואמונה מאד | 138 |
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
צמתתני קנאתי כי-שכחו דבריך צרי | 139 |
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
צרופה אמרתך מאד ועבדך אהבה | 140 |
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
צעיר אנכי ונבזה פקדיך לא שכחתי | 141 |
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
צדקתך צדק לעולם ותורתך אמת | 142 |
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
צר-ומצוק מצאוני מצותיך שעשעי | 143 |
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
צדק עדותיך לעולם הבינני ואחיה | 144 |
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
קראתי בכל-לב ענני יהוה חקיך אצרה | 145 |
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
קראתיך הושיעני ואשמרה עדתיך | 146 |
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
קדמתי בנשף ואשועה לדבריך (לדברך) יחלתי | 147 |
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
קדמו עיני אשמרות-- לשיח באמרתך | 148 |
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
קולי שמעה כחסדך יהוה כמשפטך חיני | 149 |
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
קרבו רדפי זמה מתורתך רחקו | 150 |
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
קרוב אתה יהוה וכל-מצותיך אמת | 151 |
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
קדם ידעתי מעדתיך כי לעולם יסדתם | 152 |
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
ראה-עניי וחלצני כי-תורתך לא שכחתי | 153 |
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
ריבה ריבי וגאלני לאמרתך חיני | 154 |
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
רחוק מרשעים ישועה כי חקיך לא דרשו | 155 |
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
רחמיך רבים יהוה כמשפטיך חיני | 156 |
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
רבים רדפי וצרי מעדותיך לא נטיתי | 157 |
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
ראיתי בגדים ואתקוטטה-- אשר אמרתך לא שמרו | 158 |
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
ראה כי-פקודיך אהבתי יהוה כחסדך חיני | 159 |
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
ראש-דברך אמת ולעולם כל-משפט צדקך | 160 |
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
שרים רדפוני חנם ומדבריך (ומדברך) פחד לבי | 161 |
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
שש אנכי על-אמרתך-- כמוצא שלל רב | 162 |
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
שקר שנאתי ואתעבה תורתך אהבתי | 163 |
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
שבע ביום הללתיך-- על משפטי צדקך | 164 |
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
שלום רב לאהבי תורתך ואין-למו מכשול | 165 |
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
שברתי לישועתך יהוה ומצותיך עשיתי | 166 |
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
שמרה נפשי עדתיך ואהבם מאד | 167 |
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
שמרתי פקודיך ועדתיך כי כל-דרכי נגדך | 168 |
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
תקרב רנתי לפניך יהוה כדברך הבינני | 169 |
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
תבוא תחנתי לפניך כאמרתך הצילני | 170 |
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
תבענה שפתי תהלה כי תלמדני חקיך | 171 |
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
תען לשוני אמרתך כי כל-מצותיך צדק | 172 |
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
תהי-ידך לעזרני כי פקודיך בחרתי | 173 |
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
תאבתי לישועתך יהוה ותורתך שעשעי | 174 |
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
תחי-נפשי ותהללך ומשפטך יעזרני | 175 |
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
תעיתי-- כשה אבד בקש עבדך כי מצותיך לא שכחתי | 176 |
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.