< מִשְׁלֵי 25 >

גם-אלה משלי שלמה-- אשר העתיקו אנשי חזקיה מלך-יהודה 1
Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
כבד אלהים הסתר דבר וכבד מלכים חקר דבר 2
Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
שמים לרום וארץ לעמק ולב מלכים אין חקר 3
Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
הגו סיגים מכסף ויצא לצרף כלי 4
Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
הגו רשע לפני-מלך ויכון בצדק כסאו 5
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
אל-תתהדר לפני-מלך ובמקום גדלים אל-תעמד 6
Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
כי טוב אמר-לך עלה-הנה מהשפילך לפני נדיב--אשר ראו עיניך 7
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
אל-תצא לרב מהר פן מה-תעשה באחריתה--בהכלים אתך רעך 8
usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
ריבך ריב את-רעך וסוד אחר אל-תגל 9
Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
פן-יחסדך שמע ודבתך לא תשוב 10
kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
תפוחי זהב במשכיות כסף-- דבר דבר על-אפניו 11
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
נזם זהב וחלי-כתם-- מוכיח חכם על-אזן שמעת 12
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
כצנת שלג ביום קציר--ציר נאמן לשלחיו ונפש אדניו ישיב 13
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
נשיאים ורוח וגשם אין-- איש מתהלל במתת-שקר 14
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
בארך אפים יפתה קצין ולשון רכה תשבר-גרם 15
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
דבש מצאת אכל דיך פן-תשבענו והקאתו 16
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
הקר רגלך מבית רעך פן-ישבעך ושנאך 17
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
מפיץ וחרב וחץ שנון-- איש ענה ברעהו עד שקר 18
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
שן רעה ורגל מועדת-- מבטח בוגד ביום צרה 19
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
מעדה-בגד ביום קרה--חמץ על-נתר ושר בשרים על לב-רע 20
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
אם-רעב שנאך האכלהו לחם ואם-צמא השקהו מים 21
Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
כי גחלים--אתה חתה על-ראשו ויהוה ישלם-לך 22
Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
רוח צפון תחולל גשם ופנים נזעמים לשון סתר 23
Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
טוב שבת על-פנת-גג-- מאשת מדונים (מדינים) ובית חבר 24
Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
מים קרים על-נפש עיפה ושמועה טובה מארץ מרחק 25
Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
מעין נרפש ומקור משחת-- צדיק מט לפני-רשע 26
Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
אכל דבש הרבות לא-טוב וחקר כבדם כבוד 27
Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
עיר פרוצה אין חומה-- איש אשר אין מעצר לרוחו 28
Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

< מִשְׁלֵי 25 >