< במדבר 17 >

וידבר יהוה אל משה לאמר 1
Yehova anawuza Mose kuti,
דבר אל בני ישראל וקח מאתם מטה מטה לבית אב מאת כל נשיאהם לבית אבתם--שנים עשר מטות איש את שמו תכתב על מטהו 2
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
ואת שם אהרן תכתב על מטה לוי כי מטה אחד לראש בית אבותם 3
Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
והנחתם באהל מועד--לפני העדות אשר אועד לכם שמה 4
Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
והיה האיש אשר אבחר בו--מטהו יפרח והשכתי מעלי את תלנות בני ישראל אשר הם מלינם עליכם 5
Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
וידבר משה אל בני ישראל ויתנו אליו כל נשיאיהם מטה לנשיא אחד מטה לנשיא אחד לבית אבתם--שנים עשר מטות ומטה אהרן בתוך מטותם 6
Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
וינח משה את המטת לפני יהוה באהל העדת 7
Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
ויהי ממחרת ויבא משה אל אהל העדות והנה פרח מטה אהרן לבית לוי ויצא פרח ויצץ ציץ ויגמל שקדים 8
Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
ויצא משה את כל המטת מלפני יהוה אל כל בני ישראל ויראו ויקחו איש מטהו 9
Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
ויאמר יהוה אל משה השב את מטה אהרן לפני העדות למשמרת לאות לבני מרי ותכל תלונתם מעלי ולא ימתו 10
Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
ויעש משה כאשר צוה יהוה אתו כן עשה 11
Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
ויאמרו בני ישראל אל משה לאמר הן גוענו אבדנו כלנו אבדנו 12
Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
כל הקרב הקרב אל משכן יהוה ימות האם תמנו לגוע 13
Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”

< במדבר 17 >