< איוב 41 >
תמשך לויתן בחכה ובחבל תשקיע לשנו | 1 |
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
התשים אגמן באפו ובחוח תקב לחיו | 2 |
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
הירבה אליך תחנונים אם-ידבר אליך רכות | 3 |
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
היכרת ברית עמך תקחנו לעבד עולם | 4 |
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
התשחק-בו כצפור ותקשרנו לנערותיך | 5 |
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
יכרו עליו חברים יחצוהו בין כנענים | 6 |
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
התמלא בשכות עורו ובצלצל דגים ראשו | 7 |
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
שים-עליו כפך זכר מלחמה אל-תוסף | 8 |
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
הן-תחלתו נכזבה הגם אל-מראיו יטל | 9 |
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
לא-אכזר כי יעורנו ומי הוא לפני יתיצב | 10 |
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
מי הקדימני ואשלם תחת כל-השמים לי-הוא | 11 |
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
לא- (לו-) אחריש בדיו ודבר-גבורות וחין ערכו | 12 |
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
מי-גלה פני לבושו בכפל רסנו מי יבוא | 13 |
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
דלתי פניו מי פתח סביבות שניו אימה | 14 |
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
גאוה אפיקי מגנים סגור חותם צר | 15 |
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
אחד באחד יגשו ורוח לא-יבא ביניהם | 16 |
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
איש-באחיהו ידבקו יתלכדו ולא יתפרדו | 17 |
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
עטישתיו תהל אור ועיניו כעפעפי-שחר | 18 |
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
מפיו לפידים יהלכו כידודי אש יתמלטו | 19 |
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
מנחיריו יצא עשן-- כדוד נפוח ואגמן | 20 |
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
נפשו גחלים תלהט ולהב מפיו יצא | 21 |
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
בצוארו ילין עז ולפניו תדוץ דאבה | 22 |
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
מפלי בשרו דבקו יצוק עליו בל-ימוט | 23 |
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
לבו יצוק כמו-אבן ויצוק כפלח תחתית | 24 |
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
משתו יגורו אלים משברים יתחטאו | 25 |
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
משיגהו חרב בלי תקום חנית מסע ושריה | 26 |
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
יחשב לתבן ברזל לעץ רקבון נחושה | 27 |
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
לא-יבריחנו בן-קשת לקש נהפכו-לו אבני-קלע | 28 |
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
כקש נחשבו תותח וישחק לרעש כידון | 29 |
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
תחתיו חדודי חרש ירפד חרוץ עלי-טיט | 30 |
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
ירתיח כסיר מצולה ים ישים כמרקחה | 31 |
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
אחריו יאיר נתיב יחשב תהום לשיבה | 32 |
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
אין-על-עפר משלו העשו לבלי-חת | 33 |
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
את-כל-גבה יראה הוא מלך על-כל-בני-שחץ | 34 |
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”