< איוב 40 >

ויען יהוה את-איוב ויאמר 1
Yehova anati kwa Yobu:
הרב עם-שדי יסור מוכיח אלוה יעננה 2
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
ויען איוב את-יהוה ויאמר 3
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
הן קלתי מה אשיבך ידי שמתי למו-פי 4
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
אחת דברתי ולא אענה ושתים ולא אוסיף 5
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
ויען-יהוה את-איוב מנסערה (מן סערה) ויאמר 6
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
אזר-נא כגבר חלציך אשאלך והודיעני 7
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
האף תפר משפטי תרשיעני למען תצדק 8
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
ואם-זרוע כאל לך ובקול כמהו תרעם 9
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
עדה נא גאון וגבה והוד והדר תלבש 10
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
הפץ עברות אפך וראה כל-גאה והשפילהו 11
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
ראה כל-גאה הכניעהו והדך רשעים תחתם 12
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
טמנם בעפר יחד פניהם חבש בטמון 13
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
וגם-אני אודך כי-תושע לך ימינך 14
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
הנה-נא בהמות אשר-עשיתי עמך חציר כבקר יאכל 15
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
הנה-נא כחו במתניו ואונו בשרירי בטנו 16
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
יחפץ זנבו כמו-ארז גידי פחדו ישרגו 17
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
עצמיו אפיקי נחשה גרמיו כמטיל ברזל 18
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
הוא ראשית דרכי-אל העשו יגש חרבו 19
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
כי-בול הרים ישאו-לו וכל-חית השדה ישחקו-שם 20
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
תחת-צאלים ישכב-- בסתר קנה ובצה 21
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
יסכהו צאלים צללו יסבוהו ערבי-נחל 22
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
הן יעשק נהר לא יחפוז יבטח כי-יגיח ירדן אל-פיהו 23
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
בעיניו יקחנו במוקשים ינקב-אף 24
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< איוב 40 >